< Job 41 >

1 ¿SACARÁS tú al leviathán con el anzuelo, ó con la cuerda que le echares en su lengua?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 ¿Pondrás tú garfio en sus narices, y horadarás con espinas su quijada?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 ¿Multiplicará él ruegos para contigo? ¿hablaráte él lisonjas?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 ¿Hará concierto contigo para que lo tomes por siervo perpetuo?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 ¿Jugarás tú con él como con pájaro, ó lo atarás para tus niñas?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 ¿Harán de él banquete los compañeros? ¿partiránlo entre los mercaderes?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 ¿Cortarás tú con cuchillo su cuero, ó con asta de pescadores su cabeza?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Pon tu mano sobre él; te acordarás de la batalla, y nunca más tornarás.
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 He aquí que la esperanza acerca de él será burlada: porque aun á su sola vista se desmayarán.
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 Nadie hay tan osado que lo despierte: ¿quién pues podrá estar delante de mí?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 ¿Quién me ha anticipado, para que yo restituya? [Todo lo que hay] debajo del cielo es mío.
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 Yo no callaré sus miembros, ni lo de sus fuerzas y la gracia de su disposición.
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 ¿Quién descubrirá la delantera de su vestidura? ¿quién se llegará á él con freno doble?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 ¿Quién abrirá las puertas de su rostro? Los órdenes de sus dientes espantan.
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 La gloria [de su vestido son] escudos fuertes, cerrados entre sí estrechamente.
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 El uno se junta con el otro, que viento no entra entre ellos.
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 Pegado está el uno con el otro, están trabados entre sí, que no se pueden apartar.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 Con sus estornudos encienden lumbre, y sus ojos son como los párpados del alba.
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 De su boca salen hachas de fuego; centellas de fuego proceden.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 De sus narices sale humo, como de una olla ó caldero que hierve.
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 Su aliento enciende los carbones, y de su boca sale llama.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 En su cerviz mora la fortaleza, y espárcese el desaliento delante de él.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Las partes momias de su carne están apretadas: están en él firmes, y no se mueven.
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 Su corazón es firme como una piedra, y fuerte como la muela de abajo.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 De su grandeza tienen temor los fuertes, y á causa de su desfallecimiento hacen por purificarse.
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 Cuando alguno lo alcanzare, ni espada, ni lanza, ni dardo, ni coselete durará.
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 El hierro estima por pajas, y el acero por leño podrido.
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 Saeta no le hace huir; las piedras de honda se le tornan aristas.
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Tiene toda arma por hojarascas, y del blandir de la pica se burla.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Por debajo [tiene] agudas conchas; Imprime [su] agudez en el suelo.
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 Hace hervir como una olla la profunda mar, y tórnala como una olla de ungüento.
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 En pos de sí hace resplandecer la senda, que parece que la mar es cana.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 No hay sobre la tierra su semejante, hecho para nada temer.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Menosprecia toda cosa alta: es rey sobre todos los soberbios.
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< Job 41 >