< Job 27 >
1 Y REASUMIÓ Job su discurso, y dijo:
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Vive Dios, el cual ha apartado mi causa, y el Omnipotente, que amargó el alma mía,
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
3 Que todo el tiempo que mi alma estuviere en mí, y [hubiere] hálito de Dios en mis narices,
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
4 Mis labios no hablarán iniquidad, ni mi lengua pronunciará engaño.
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
5 Nunca tal acontezca que yo os justifique: hasta morir no quitaré de mí mi integridad.
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
6 Mi justicia tengo asida, y no la cederé: no [me] reprochará mi corazón en el tiempo de mi vida.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
7 Sea como el impío mi enemigo, y como el inicuo mi adversario.
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
8 Porque ¿cuál es la esperanza del hipócrita, por mucho que hubiere robado, cuando Dios arrebatare su alma?
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
9 ¿Oirá Dios su clamor cuando la tribulación sobre él viniere?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
10 ¿Deleitaráse en el Omnipotente? ¿invocará á Dios en todo tiempo?
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
11 Yo os enseñaré en orden á la mano de Dios: no esconderé lo que hay para con el Omnipotente.
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 He aquí que todos vosotros lo habéis visto: ¿por qué pues os desvanecéis con fantasía?
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
13 Esta es para con Dios la suerte del hombre impío, y la herencia que los violentos han de recibir del Omnipotente.
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 Si sus hijos fueren multiplicados, serán para el cuchillo; y sus pequeños no se hartarán de pan;
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 Los que le quedaren, en muerte serán sepultados; y no llorarán sus viudas.
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 Si amontonare plata como polvo, y si preparare ropa como lodo;
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 Habrála él preparado, mas el justo se vestirá, y el inocente repartirá la plata.
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 Edificó su casa como la polilla, y cual cabaña que el guarda hizo.
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 El rico dormirá, mas no será recogido: abrirá sus ojos, mas él no será.
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Asirán de él terrores como aguas: torbellino lo arrebatará de noche.
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 Lo antecogerá el solano, y partirá; y tempestad lo arrebatará del lugar suyo.
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
22 [Dios] pues descargará sobre él, y no perdonará: hará él por huir de su mano.
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 Batirán sus manos sobre él, y desde su lugar le silbarán.
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”