< Job 23 >

1 Y RESPONDIÓ Job, y dijo:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Hoy también hablaré con amargura; que es más grave mi llaga que mi gemido.
“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
3 ¡Quién me diera el saber dónde hallar á Dios! yo iría hasta su silla.
Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
4 Ordenaría juicio delante de él, y henchiría mi boca de argumentos.
Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
5 Yo sabría lo que él me respondería, y entendería lo que me dijese.
Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
6 ¿Pleitearía conmigo con grandeza de fuerza? No: antes él la pondría en mí.
Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
7 Allí el justo razonaría con él: y escaparía para siempre de mi juez.
Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
8 He aquí yo iré al oriente, y no lo [hallaré]; y al occidente, y no lo percibiré:
“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
9 Si al norte él obrare, yo no lo veré; al mediodía se esconderá, y no lo veré.
Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
10 Mas él conoció mi camino: probaráme, y saldré como oro.
Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
11 Mis pies tomaron su rastro; guardé su camino, y no me aparté.
Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
12 Del mandamiento de sus labios nunca me separé; guardé las palabras de su boca más que mi comida.
Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
13 Empero si él [se determina] en una cosa, ¿quién lo apartará? Su alma deseó, é hizo.
“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
14 El pues acabará lo que ha determinado de mí: y muchas cosas como estas hay en él.
Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
15 Por lo cual yo me espanto en su presencia: consideraré, y temerélo.
Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
16 Dios ha enervado mi corazón, y hame turbado el Omnipotente.
Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
17 ¿Por qué no fuí yo cortado delante de las tinieblas, y cubrió con oscuridad mi rostro?
Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

< Job 23 >