< Jeremías 46 >
1 PALABRA de Jehová que fué á Jeremías profeta, contra las gentes.
Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.
2 En orden á Egipto: contra el ejército de Faraón Nechâo rey de Egipto, que estaba cerca del río Eufrates en Carchêmis, al cual hirió Nabucodonosor rey de Babilonia el año cuarto de Joacim hijo de Josías, rey de Judá.
Kunena za Igupto: Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,
3 Aparejad escudo y pavés, y venid á la guerra.
anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo, ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!
4 Uncid caballos, y subid, vosotros los caballeros, y poneos con capacetes; limpiad las lanzas, vestíos de lorigas.
Mangani akavalo, ndipo kwerani inu okwerapo! Khalani pa mzere mutavala zipewa! Nolani mikondo yanu, valani malaya anu ankhondo!
5 ¿Por qué los vi medrosos, tornando atrás? y sus valientes fueron deshechos, y huyeron á más huir sin volver á mirar atrás: miedo de todas partes, dice Jehová.
Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani? Achita mantha akubwerera, ankhondo awo agonjetsedwa. Akuthawa mofulumirapo osayangʼananso mʼmbuyo, ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,” akutero Yehova.
6 No huya el ligero, ni el valiente escape; al aquilón junto á la ribera del Eufrates tropezaron y cayeron.
Waliwiro sangathe kuthawa ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka. Akunka napunthwa ndi kugwa kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.
7 ¿Quién es éste que como río sube, y cuyas aguas se mueven como ríos?
“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo, ngati mtsinje wa madzi amkokomo?
8 Egipto como río se hincha, y las aguas se mueven como ríos, y dijo: Subiré, cubriré la tierra, destruiré la ciudad y los que en ella moran.
Igupto akusefukira ngati Nailo, ngati mitsinje ya madzi amkokomo. Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi; ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’
9 Subid, caballos, y alborotaos, carros; y salgan los valientes: los de Cus y los de Phut que toman escudo, y los de Lut que toman y entesan arco.
Tiyeni, inu akavalo! Thamangani inu magaleta! Tulukani, inu ankhondo, ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango, ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.
10 Mas ese día será á Jehová Dios de los ejércitos día de venganza, para vengarse de sus enemigos: y la espada devorará y se hartará, y se embriagará de la sangre de ellos: porque matanza será á Jehová, Dios de los ejércitos, en tierra del aquilón junto al río Eufrates.
Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse; tsiku lolipsira, lolipsira adani ake. Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi, lidzaledzera ndi magazi. Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
11 Sube á Galaad, y toma bálsamo, virgen hija de Egipto: por demás multiplicarás medicinas; no hay cura para ti.
“Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala iwe namwali Igupto. Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira; palibe mankhwala okuchiritsa.
12 Las gentes oyeron tu afrenta, y tu clamor hinchió la tierra: porque fuerte se encontró con fuerte, y cayeron ambos juntos.
Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako; kulira kwako kwadzaza dziko lapansi. Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana, onse awiri agwa pansi limodzi.”
13 Palabra que habló Jehová á Jeremías profeta acerca de la venida de Nabucodonosor, rey de Babilonia, para herir la tierra de Egipto:
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:
14 Denunciad en Egipto, y haced saber en Migdol: haced saber también en Noph y en Taphnes; decid: Para, y apercíbete; porque espada ha de devorar tu comarca.
“Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli. Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi. Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza, chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’
15 ¿Por qué ha sido derribado tu fuerte? no se pudo tener, porque Jehová lo rempujó.
Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa? Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.
16 Multiplicó los caídos, y cada uno cayó sobre su compañero, y dijeron: Levántate y volvámonos á nuestro pueblo, y á la tierra de nuestro nacimiento, de delante de la espada vencedora.
Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa. Aliyense akuwuza mnzake kuti, ‘Tiyeni tibwerere kwathu, ku dziko kumene tinabadwira, tithawe lupanga la adani athu.’
17 Allí gritaron: Faraón rey de Egipto, [rey de] revuelta: dejó pasar el tiempo señalado.
Kumeneku iwo adzafuwula kuti, ‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti, Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’
18 Vivo yo, dice el Rey, cuyo nombre es Jehová de los ejércitos, que como Tabor entre los montes, y como Carmelo en la mar, así vendrá.
“Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse, “wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena, ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.
19 Hazte vasos de transmigración, moradora hija de Egipto; porque Noph será por yermo, y será asolada hasta no quedar morador.
Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo inu anthu a ku Igupto, pakuti Mefisi adzasanduka chipululu ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.
20 Becerra hermosa Egipto; [mas] viene destrucción, del aquilón viene.
“Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola, koma chimphanga chikubwera kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.
21 Sus soldados también en medio de ella como engordados becerros: que también ellos se volvieron, huyeron todos sin pararse: porque vino sobre ellos el día de su quebrantamiento, el tiempo de su visitación.
Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye ali ngati ana angʼombe onenepa. Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi. Palibe amene wachirimika. Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira; ndiyo nthawi yowalanga.
22 Su voz saldrá como de serpiente; porque con ejército vendrán, y con hachas vienen á ella como cortadores de leña.
Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa pamene adani abwera ndi zida zawo, abwera ndi nkhwangwa ngati anthu odula mitengo.
23 Cortaron su bosque, dice Jehová, porque no podrán ser contados; porque serán más que langostas, ni tendrán número.
Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,” akutero Yehova, “ngakhale kuti ndi yowirira. Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe, moti sangatheke kuwerengeka.
24 Avergonzóse la hija de Egipto; entregada será en mano del pueblo del aquilón.
Anthu a ku Igupto achita manyazi atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”
25 Jehová de los ejércitos, Dios de Israel, ha dicho: He aquí que yo visito el pueblo de Amón de No, y á Faraón y á Egipto, y á sus dioses y á sus reyes; así á Faraón como á los que en él confían.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira.
26 Y entregarélos en mano de los que buscan su alma, y en mano de Nabucodonosor rey de Babilonia, y en mano de sus siervos: mas después será habitada como en los días pasados, dice Jehová.
Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.
27 Y tú no temas, siervo mío Jacob, y no desmayes, Israel; porque he aquí que yo te salvo de lejos, y á tu simiente de la tierra de su cautividad. Y volverá Jacob, y descansará y será prosperado, y no habrá quien lo espante.
“Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha; usataye mtima, iwe Israeli. Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali, ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere, ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.
28 Tú, siervo mío Jacob, no temas, dice Jehová; porque yo soy contigo: porque haré consumación en todas las gentes á las cuales te habré echado; mas en ti no haré consumación, sino que te castigaré con juicio, y no te talaré del todo.
Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova. “Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu a ku mayiko kumene ndakupirikitsira, Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu. Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera; sindidzakulekerera osakulanga.”