< Salmos 88 >
1 Jehová Dios de mi salud, día y noche clamo delante de ti.
Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
2 Entre delante de ti mi oración: inclina tu oído a mi clamor.
Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
3 Porque mi alma está harta de males: y mi vida ha llegado a la sepultura. (Sheol )
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol )
4 Soy contado con los que descienden al sepulcro: soy como hombre sin fuerza;
Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
5 Librado entre los muertos. Como los matados que duermen en el sepulcro: que no te acuerdas más de ellos, y que son cortados de tu mano.
Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
6 Hásme puesto en el hoyo profundo: en tinieblas, en honduras.
Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
7 Sobre mí se ha acostado tu ira: y con todas tus ondas me has afligido. (Selah)
Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
8 Has alejado de mí mis conocidos: hásme puesto a ellos por abominaciones: estoy encerrado, y no saldré.
Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
9 Mis ojos enfermaron a causa de mi aflicción: te he llamado, o! Jehová, cada día he extendido a ti mis manos.
maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 ¿Harás milagro a los muertos? ¿Levantarse han los muertos para alabarte? (Selah)
Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
11 ¿Será contada en el sepulcro tu misericordia? ¿tu verdad en la perdición?
Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 ¿Será conocida en las tinieblas tu maravilla? ¿y tu justicia en la tierra del olvido?
Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
13 Y yo a ti, o! Jehová, he clamado: y de mañana te previno mi oración.
Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 ¿Por qué, o! Jehová, desechas a mi alma? ¿ por qué escondes tu rostro de mí?
Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
15 Yo soy afligido y menesteroso: desde la mocedad he llevado tus temores, he estado medroso.
Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 Sobre mí han pasado tus iras; tus espantos me han cortado.
Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
17 Hánme rodeado como aguas de continuo: hánme cercado a una.
Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
18 Has alejado de mí el amigo y el compañero; y mis conocidos en las tinieblas.
Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.