< Salmos 34 >
1 Bendeciré a Jehová en todo tiempo; siempre será su alabanza en mi boca.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 En Jehová se alabará mi alma; oirán los mansos, y alegrarse han.
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Engrandecéd a Jehová, conmigo; y ensalcemos su nombre a una.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 Busqué a Jehová, y él me oyó; y de todos mis miedos me libró.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 Miraron a él, y fueron alumbrados; y sus rostros no se avergonzaron.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 Este pobre llamó, y Jehová le oyó, y de todas sus angustias le escapó.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 El ángel de Jehová asienta campo en derredor de los que le temen, y los defiende.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 Gustád, y ved que es bueno Jehová; dichoso el varón que confiará en él.
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Teméd a Jehová sus santos; porque no hay falta para los que le temen.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Los leoncillos empobrecieron, y tuvieron hambre; y los que buscan a Jehová, no tendrán falta de ningún bien.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Veníd, hijos, oídme; temor de Jehová os enseñaré.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 ¿Quién es el varón que desea vida, qué codicia días para ver bien?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Guarda tu lengua de mal, y tus labios de hablar engaño.
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Apártate del mal, y haz el bien; inquiere la paz, y síguela.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 Los ojos de Jehová están sobre los justos; y sus oídos al clamor de ellos.
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 La ira de Jehová contra los que mal hacen, para cortar de la tierra la memoria de ellos.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 Clamaron, y Jehová los oyó: y de todas sus angustias los escapó.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Cercano está Jehová a los quebrantados de corazón: y a los molidos de espíritu salvará.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Muchos son los males del justo: y de todos ellos le escapará Jehová.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Guardando todos sus huesos; uno de ellos no será quebrantado.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 Matará al malo la maldad; y los que aborrecen al justo serán asolados.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 Redime Jehová la vida de sus siervos; y no serán asolados todos los que en él confían.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.