< Salmos 116 >

1 Amé a Jehová, porque ha oído mi voz: mis ruegos.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Porque ha inclinado su oído a mí; y en mis días le llamaré,
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Rodeáronme los dolores de la muerte, las angustias del sepulcro me hallaron: angustia y dolor había hallado: (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 Y llamé el nombre de Jehová: Escapa ahora mi alma, o! Jehová.
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Clemente es Jehová y justo, y misericordioso nuestro Dios.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 Guarda a los sencillos Jehová: yo estaba debilitado y salvóme.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Vuelve, o! alma mía, a tu reposo; porque Jehová te ha hecho bien.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Porque has librado mi alma de la muerte, mis ojos de las lágrimas, mis pies del rempujón.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 Andaré delante de Jehová en las tierras de los vivos.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Creí, por tanto hablé: y fui afligido en gran manera.
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 Y dije en mi apresuramiento: Todo hombre es mentiroso.
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 ¿Qué pagaré a Jehová por todos sus beneficios sobre mí?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 El vaso de saludes tomaré; e invocaré el nombre de Jehová.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Ahora pagaré mis votos a Jehová delante de todo su pueblo.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Estimada es en los ojos de Jehová la muerte de sus piadosos.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Así es, o! Jehová; porque yo soy tu siervo, yo soy tu siervo, hijo de tu sierva, tú rompiste mis prisiones.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 A ti sacrificaré sacrificio de alabanza; y el nombre de Jehová invocaré.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Ahora pagaré mis votos a Jehová delante de todo su pueblo;
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 En los patios de la casa de Jehová; en medio de ti, o! Jerusalem. Alelu- Jah.
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Salmos 116 >