< Proverbios 5 >

1 Hijo mío está atento a mi sabiduría, y a mi inteligencia inclina tu oído:
Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
2 Para que guardes mis consejos; y tus labios conserven la ciencia.
kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
3 Porque los labios de la mujer extraña destilan panal de miel; y su paladar es más suave que el aceite:
Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
4 Mas su fin es amargo como el ajenjo; agudo como espada de dos filos.
koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
5 Sus pies descienden a la muerte: sus pasos sustentan el sepulcro. (Sheol h7585)
Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol h7585)
6 Si no pesares el camino de vida, sus caminos son instables: no los conocerás.
Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
7 Ahora pues, hijos, oídme, y no os apartéis de las razones de mi boca.
Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
8 Aleja de ella tu camino; y no te acerques a la puerta de su casa.
Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
9 Porque no des a los extraños tu honor; y tus años a cruel.
kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
10 Porque no se harten los extraños de tu fuerza; y tus trabajos estén en casa del extraño:
kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
11 Y gimas en tus postrimerías, cuando se consumiere tu carne y tu cuerpo,
Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
12 Y digas: ¿Cómo aborrecí el castigo; y mi corazón menospreció la reprensión,
Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
13 Y no oí la voz de los que me castigaban; y a los que me enseñaban no incliné mi oído?
Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
14 Poco se faltó para que no cayese en todo mal, en medio de la compañía y de la congregación.
Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
15 Bebe el agua de tu cisterna, y las corrientes de tu pozo.
Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
16 Derrámense por de fuera tus fuentes: en las plazas los ríos de tus aguas.
Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
17 Sean para ti solo, y no para los extraños contigo.
Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
18 Será bendito tu manadero; y alégrate de la mujer de tu mocedad.
Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
19 Cierva amada, y graciosa cabra; sus pechos te hartarán en todo tiempo; y de su amor andarás ciego de continuo.
Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
20 ¿Y por qué andarás ciego, hijo mío, con la ajena, y abrazarás el seno de la extraña?
Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
21 Pues que los caminos del hombre están delante de los ojos de Jehová, y él pesa todas sus veredas.
Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
22 Sus iniquidades prenderán al impío; y con las cuerdas de su pecado será detenido.
Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
23 Él morirá sin castigo; y por la multitud de su locura errará.
Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.

< Proverbios 5 >