< Proverbios 3 >
1 Hijo mío, no te olvides de mi ley; y tu corazón guarde mis mandamientos:
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 Porque longura de días, y años de vida, y paz te aumentarán.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Misericordia, y verdad no te desamparen: átalas a tu cuello, escríbelas en la tabla de tu corazón;
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Y hallarás gracia y buena opinión en los ojos de Dios, y de los hombres.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Fíate de Jehová de todo tu corazón; y no estribes en tu prudencia.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Reconócele en todos tus caminos; y él enderezará tus veredas.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 No seas sabio en tu opinión: teme a Jehová, y apártate del mal:
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 Porque será medicina a tu ombligo, y tuétano a tus huesos.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Honra a Jehová de tu sustancia; y de las primicias de todos tus frutos:
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 Y serán llenos tus alfolíes de hartura; y tus lagares reventarán de mosto.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 No deseches, hijo mío, el castigo de Jehová: ni te fatigues de su corrección:
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Porque Jehová al que ama, y quiere, como el padre al hijo, a ese castiga.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Bienaventurado el hombre que halló la sabiduría; y que saca a luz la inteligencia.
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 Porque su mercadería es mejor que la mercadería de la plata; y sus frutos, más que el oro fino.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Más preciosa es que las piedras preciosas; y todo lo que puedes desear, no se puede comparar a ella.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Longura de días trae en su mano derecha: en su izquierda, riquezas y honra.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Sus caminos son caminos deleitosos; y todas sus veredas, paz.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Esta es el árbol de vida a los que asen de ella; y los que la sustentan, son bienaventurados.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Jehová con sabiduría fundó la tierra: afirmó los cielos con inteligencia.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Con su ciencia se partieron los abismos; y los cielos destilan el rocío.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Hijo mío, no se aparten estas cosas de tus ojos: guarda la ley, y el consejo;
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 Y serán vida a tu alma, y gracia a tu cuello.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Entonces caminarás por tu camino confiadamente; y tu pie no tropezará.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Cuando te acostares, no habrás temor; y acostarte has, y tu sueño será suave.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 No habrás temor del pavor repentino, ni de la ruina de los impíos, cuando viniere.
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 Porque Jehová será tu confianza; y el guardará tu pie, porque no seas tomado.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 No detengas el bien de sus dueños, cuando tuvieres poder para hacerlo.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 No digas a tu prójimo: Vé, y vuelve, y mañana te daré, cuando tienes contigo.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 No pienses mal contra tu prójimo, estando él confiado de ti.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 No pleitées con alguno sin razón, si él no te ha malgalardonado.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 No tengas envidia al hombre injusto: ni escojas alguno de sus caminos:
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Porque el perverso es abominado de Jehová; y con los rectos es su secreto.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Maldición de Jehová está en la casa del impío; mas a la morada de los justos bendecirá.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Ciertamente él escarnecerá a los escarnecedores; y a los humildes dará gracia.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Los sabios heredarán la honra; y los insensatos sostendrán deshonra.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.