< Proverbios 13 >

1 El hijo sabio recibe la enseñanza del padre: mas el burlador no escucha la reprensión.
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 Del fruto de la boca el hombre comerá bien: mas el alma de los prevaricadores, mal.
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 El que guarda su boca, guarda su alma: mas el que abre sus labios tendrá calamidad.
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 Desea, y nada alcanza el alma del perezoso: mas el alma de los diligentes será engordada.
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
5 El justo aborrecerá la palabra de mentira; mas el impío se hace hediondo, y confuso.
Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6 La justicia guarda al de perfecto camino; mas la impiedad trastornará al pecador.
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 Hay algunos que se hacen ricos, y no tienen nada; y otros, que se hacen pobres, y tienen muchas riquezas.
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 La redención de la vida del hombre son sus riquezas; y el pobre no escucha la reprensión.
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 La luz de los justos se alegrará: mas la candela de los impíos se apagará.
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 Ciertamente la soberbia parirá contienda: mas con los avisados es la sabiduría.
Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 Las riquezas de vanidad se disminuirán: mas el que allega con su mano, multiplicará.
Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 La esperanza que se alarga, es tormento del corazón: mas árbol de vida es el deseo cumplido.
Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 El que menosprecia la palabra, perecerá por ello: mas el que teme el mandamiento, será pagado.
Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 La ley al sabio es manadero de vida para apartarse de los lazos de la muerte.
Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 El buen entendimiento conciliará gracia: mas el camino de los prevaricadores es duro.
Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 Todo hombre cuerdo hace con sabiduría: mas el insensato manifestará fatuidad.
Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 El mal mensajero caerá en mal: mas el mensajero fiel es medicina.
Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 Pobreza y vergüenza tendrá el que menospreciare la enseñanza: mas el que guarda la corrección, será honrado.
Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 El deseo cumplido deleita al alma: mas apartarse del mal, es abominación a los insensatos.
Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 El que anda con los sabios, será sabio: mas el que se allega a los insensatos, será quebrantado.
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 Mal perseguirá a los pecadores: mas a los justos bien será pagado.
Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 El bueno dejará herederos a los hijos de los hijos; y el haber del pecador para el justo está guardado.
Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 En el barbecho de los pobres hay mucho pan: mas piérdese por falta de juicio.
Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 El que detiene el castigo, a su hijo aborrece: mas el que le ama, madruga a castigarle.
Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 El justo come hasta que su alma se harta: mas el vientre de los impíos tendrá necesidad.
Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

< Proverbios 13 >