< Nehemías 7 >

1 Y fue, que como el muro fue edificado, y asenté las puertas, y fueron señalados porteros, y cantores, y Levitas,
Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
2 Mandé a Janani mi hermano, y a Jananías príncipe del palacio en Jerusalem: porque este era, como varón de verdad y temeroso de Dios, sobre muchos:
Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
3 Y díjeles: No se abran las puertas de Jerusalem hasta que el sol caliente: y aun ellos presentes, cierren las puertas, y atrancád. Y señalé guardias de los moradores de Jerusalem, cada uno en su guardia, y cada uno delante de su casa.
Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
4 Y la ciudad era ancha de espacio y grande, y poco pueblo dentro de ella; que no había aun casas edificadas.
Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
5 Mas puso Dios en mi corazón que juntase los principales, y los magistrados, y el pueblo, para que fuesen empadronados por el orden de los linajes; y hallé el libro de la genealogía de los que habían subido antes, y hallé escrito en él:
Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6 Estos son los hijos de la provincia, que subieron de la cautividad de la transmigración, que hizo pasar Nabucodonosor rey de Babilonia, los cuales volvieron a Jerusalem y a Judá, cada uno a su ciudad.
Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
7 Los cuales vinieron con Zorobabel, Jesuá, Nehemías, Azarías, Raamías, Nahamani, Mardoqueo, Bilsán, Misperet, Biguai, Nehum, Baana. La cuenta de los varones del pueblo de Israel:
Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
8 Los hijos de Faros, dos mil y ciento y setenta y dos.
Zidzukulu za Parosi 2,172
9 Los hijos de Safatías, trescientos y setenta y dos.
Zidzukulu za Sefatiya 372
10 Los hijos de Area, seiscientos y cincuenta y dos.
Zidzukulu za Ara 652
11 Los hijos de Pahat-moab, de los hijos de Jesuá, y de Joab, dos mil y ochocientos y diez y ocho.
Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
12 Los hijos de Elam, mil y doscientos y cincuenta y cuatro.
Zidzukulu za Elamu 1,254
13 Los hijos de Zattu, ochocientos y cuarenta y cinco.
Zidzukulu za Zatu 845
14 Los hijos de Zecai, setecientos y sesenta.
Zidzukulu za Zakai 760
15 Los hijos de Binui, seiscientos y cuarenta y ocho.
Zidzukulu za Binuyi 648
16 Los hijos de Bebai, seiscientos y veinte y ocho.
Zidzukulu za Bebai 628
17 Los hijos de Azgad, dos mil y seiscientos y veinte y dos.
Zidzukulu za Azigadi 2,322
18 Los hijos de Adonicam, seiscientos y sesenta y siete.
Zidzukulu za Adonikamu 667
19 Los hijos de Biguai, dos mil y sesenta y siete.
Zidzukulu za Abigivai 2,067
20 Los hijos de Addín, seiscientos y cincuenta y cinco.
Zidzukulu za Adini 655
21 Los hijos de Ater, de Ezequías, noventa y ocho.
Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
22 Los hijos de Hasum, trescientos y veinte y ocho.
Zidzukulu za Hasumu 328
23 Los hijos de Besaí, trescientos y veinte y cuatro.
Zidzukulu za Bezayi 324
24 Los hijos de Harif, ciento y doce.
Zidzukulu za Harifu 112
25 Los hijos de Gabaón, noventa y cinco.
Zidzukulu za Gibiyoni 95.
26 Los varones de Belén y de Netofa, ciento y ochenta y ocho.
Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
27 Los varones de Anatot, ciento y veinte y ocho.
Anthu a ku Anatoti 128
28 Los varones de Bet-azmavet, cuarenta y dos.
Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
29 Los varones de Cariat-jarim, Quefira y Beerot, setecientos y cuarenta y tres.
Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
30 Los varones de Rama y de Gabaa, seiscientos y veinte y uno.
Anthu a ku Rama ndi Geba 621
31 Los varones de Macmas, ciento y veinte y dos.
Anthu a ku Mikimasi 122
32 Los varones de Bet-el y de Ai, ciento y veinte y tres.
Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
33 Los varones de la otra Nebo, cincuenta y dos.
Anthu a ku Nebo winayo 52
34 Los hijos de la otra Elam, mil y doscientos y cincuenta y cuatro.
Ana a Elamu wina 1,254
35 Los hijos de Harim, trescientos y veinte.
Zidzukulu za Harimu 320
36 Los hijos de Jericó, trescientos y cuarenta y cinco.
Zidzukulu za Yeriko 345
37 Los hijos de Lod, Hadid, y de Ono, siete cientos y veinte y uno.
Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
38 Los hijos de Senaa, tres mil y novecientos y treinta.
Zidzukulu za Senaya 3,930.
39 Sacerdotes: Los hijos de Jedaias de la casa de Jesuá, novecientos y setenta y tres.
Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
40 Los hijos de Immer, mil y cincuenta y dos.
Zidzukulu za Imeri 1,052
41 Los hijos de Fasur, mil y doscientos y cuarenta y siete.
Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
42 Los hijos de Harim, mil y diez y siete.
Zidzukulu za Harimu 1,017.
43 Levitas: Los hijos de Jesuá, de Cadmiel, de los hijos de Odvia, setenta y cuatro.
Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
44 Cantores: Los hijos de Asaf, ciento y cuarenta y ocho.
Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
45 Porteros: Los hijos de Sellum, los hijos de Ater, los hijos de Talmón, los hijos de Accub, los hijos de Hatita, los hijos de Sobai, ciento y treinta y ocho.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
46 Natineos: Los hijos de Siha, los hijos de Hasufa, los hijos de Tabaot,
Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
47 Los hijos de Ceros, los hijos de Sea, los hijos de Padón,
Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
48 Los hijos de Lebana, los hijos de Hagaba, los hijos de Salmai,
Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
49 Los hijos de Hanán, los hijos de Giddel, los hijos de Gahar,
Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
50 Los hijos de Reaia, los hijos de Resín, los hijos de Necoda,
Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
51 Los hijos de Gazzam, los hijos de Uzza, los hijos de Fasea,
Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
52 Los hijos de Besai, los hijos de Meunim, los hijos de Nefisesim,
Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
53 Los hijos de Bacbuc, los hijos de Hacufa, los hijos de Harur,
Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
54 Los hijos de Baslit, los hijos de Mehida, los hijos de Harsa,
Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
55 Los hijos de Barcos, los hijos de Sísera, los hijos de Tama,
Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
56 Los hijos de Nesia, los hijos de Hatifa.
Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
57 Los hijos de los siervos de Salomón: los hijos de Sotai, los hijos de Soforet, los hijos de Perida,
Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
58 Los hijos de Jaala, los hijos de Darcón, los hijos de Giddel,
zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
59 Los hijos de Safatías, los hijos de Hatil, los hijos de Poqueret de Hasbaim, los hijos de Amón.
zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
60 Todos los Natineos, e hijos de los siervos de Salomón, trescientos y noventa y dos.
Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
61 Y estos son los que subieron de Tel-mela, Tel-harsa, Querub, Addón, e Immer, los cuales no pudieron mostrar la casa de sus padres, y su linaje, si eran de Israel:
Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62 Los hijos de Delaia, los hijos de Tobías, los hijos de Necoda, seiscientos y cuarenta y dos.
Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
63 Y de los sacerdotes: los hijos de Hobaias, los hijos de Haccos, los hijos de Berzellai, que tomó mujer de las hijas de Berzellai Galaadita, y se llamó del nombre de ellas.
Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
64 Estos buscaron su escritura de genealogías, y no fueron hallados, y fueron echados del sacerdocio.
Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
65 Y díjoles el Tirsata, que no comiesen de la santidad de las santidades, hasta que hubiese sacerdote con Urim y Tumim.
Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66 Toda la congregación como un varón, fueron cuarenta y dos mil y trescientos y sesenta,
Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
67 Sin sus siervos y siervas, los cuales eran siete mil y trescientos y treinta y siete: y entre ellos había cantores y cantoras, doscientos y cuarenta y cinco.
Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
68 Sus caballos, siete cientos y treinta y seis: sus mulos, doscientos y cuarenta y cinco:
Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69 Camellos, cuatrocientos y treinta y cinco: asnos, seis mil y siete cientos y veinte.
Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70 Y algunos de los príncipes de las familias dieron para la obra: el Tirsata dio para el tesoro mil dracmas de oro; tazones cincuenta; vestimentos sacerdotales quinientos y treinta.
Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
71 Y de los príncipes de las familias dieron para el tesoro de la obra veinte mil dracmas de oro, y dos mil y doscientas libras de plata.
Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
72 Y lo que dio el resto del pueblo fue veinte mil dracmas de oro, y dos mil libras de plata, y vestiduras sacerdotales sesenta y siete.
Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73 Y habitaron los sacerdotes y los Levitas, y los porteros, y los cantores, y los del pueblo, y los Natineos, y todo Israel, en sus ciudades: y venido el mes séptimo, los hijos de Israel estaban en sus ciudades.
Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.

< Nehemías 7 >