< Job 30 >

1 Mas ahora los más mozos de días que yo, se rien de mí, cuyos padres yo desdeñara de ponerlos con los perros de mi ganado,
“Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
2 Porque ¿para qué había yo menester la fuerza de sus manos, en los cuales pereció el tiempo?
Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
3 Por causa de la pobreza y de la hambre solos: que huían a la soledad, al lugar tenebroso, asolado y desierto.
Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
4 Que cogían malvas entre los árboles, y raíces de enebros para calentarse.
Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
5 Eran echados de entre las gentes, y todos les daban grita como a ladrón.
Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
6 Que habitaban en las barrancas de los arroyos, en las cavernas de la tierra, y en las piedras.
Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
7 Que bramaban entre las matas, y se congregaban debajo de las espinas.
Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
8 Hijos de viles, y hombres sin nombre: mas bajos que la misma tierra.
Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
9 Y ahora yo soy su canción, y soy hecho a ellos refrán.
“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
10 Abomínanme, aléjanse de mí; y aun de mi rostro no detuvieron su saliva.
Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
11 Porque Dios desató mi cuerda, y me afligió; y quitaron el freno delante de mi rostro.
Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
12 A la mano derecha se levantaron los muchachos; rempujaron mis pies, y pisaron sobre mí las sendas de su contrición.
Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
13 Mi senda derribaron: aprovecháronse de mi quebrantamiento; contra los cuales no hubo ayudador.
Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
14 Vinieron como por portillo ancho: revolviéronse por mi calamidad.
Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
15 Turbaciones se convirtieron sobre mí: combatieron como un viento mi voluntad, y mi salud como nube que pasa.
Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
16 Y ahora mi alma está derramada en mí: días de aflicción me han comprendido.
“Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
17 De noche taladra sobre mí mis huesos, y mis pulsos no reposan.
Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
18 Con la grandeza de la fuerza del dolor mi vestidura es mudada; cíñeme como el collar de mi ropa.
Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
19 Derribóme en el lodo, y soy semejante al polvo, y a la ceniza.
Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
20 Clamo a ti, y no me oyes: me presento, y no me echas de ver.
“Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
21 Háste tornado cruel para mí: con la fortaleza de tu mano me amenazas.
Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
22 Levantásteme, e hicísteme cabalgar sobre el viento, y derretiste en mí el ser.
Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
23 Porque yo conozco que me tornas a la muerte, y a la casa determinada a todo viviente.
Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
24 Mas él no extenderá la mano contra el sepulcro; ¿clamarán los sepultados cuando él los quebrantare?
“Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
25 ¿No lloré yo al afligido, y mi alma no se entristeció sobre el menesteroso?
Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
26 Cuando esperaba el bien, entonces me vino el mal; y cuando esperaba la luz, vino la oscuridad.
Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
27 Mis entrañas hierven, y no reposan: previniéronme días de aflicción.
Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
28 Denegrido anduve, y no por el sol: levantéme en la congregación, y clamé.
Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
29 Hermano fui de los dragones, y compañero de las hijas del avestruz.
Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
30 Mi cuero está denegrido sobre mí, y mis huesos se secaron con sequedad.
Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
31 Y mi arpa se tornó en luto, y mi órgano en voz de lamentantes.
Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.

< Job 30 >