< Job 27 >
1 Y tornó Job a tomar su parábola, y dijo:
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Vive el Dios que me quitó mi derecho; y el Omnipotente, que amargó mi alma:
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
3 Que todo el tiempo que mi alma estuviere en mí, y hubiere resuello de Dios en mis narices,
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
4 Mis labios no hablarán iniquidad: ni mi lengua pronunciará engaño.
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
5 Nunca tal me acontezca, que yo os justifique: hasta morir no quitaré mi integridad de mí.
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
6 Mi justicia tengo asida, y no la aflojaré, no se avergonzará mi corazón de mis días.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
7 Sea como el impío mi enemigo, y como el inicuo mi adversario.
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
8 Porque ¿qué es la esperanza del hipócrita, si mucho hubiere robado, cuando Dios arrebatare su alma?
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
9 ¿Oirá Dios su clamor, cuando viniere sobre él la tribulación?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
10 ¿Se deleitará en el Omnipotente? ¿llamará a Dios en todo tiempo?
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
11 Yo os enseñaré lo que está en la mano de Dios: no esconderé lo que está acerca del Omnipotente.
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 He aquí, que todos vosotros lo habéis visto: ¿por qué pues os desvanecéis con vanidad?
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
13 Esta es la suerte del hombre impío acerca de Dios, y la herencia que los violentos han de recibir del Omnipotente.
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 Si sus hijos fueren multiplicados, serán para la espada, y sus pequeños no se hartarán de pan.
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 Los que de ellos quedaren, en muerte serán sepultados, y sus viudas no llorarán.
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 Sí amontonare plata como polvo, y si aparejare ropa como lodo:
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 Aparejará, mas el justo se vestirá, y el inocente repartirá la plata.
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 Edificó su casa como la polilla, y como cabaña que hizo alguna guarda.
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 El rico dormirá, mas no será recogido: abrirá sus ojos, y no verá a nadie.
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Asirán de él terrores como aguas: torbellino le arrebatará de noche.
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 Tomarle ha solano, e irse ha: y tempestad le arrebatará de su lugar.
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
22 Y echará sobre él, y no perdonará: huyendo huirá de su mano.
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 Batirá sus manos sobre él, y desde su lugar le silbará.
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”