< Job 23 >

1 Y respondió Job, y dijo:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Hoy también hablaré con amargura, y será más grave mi llaga que mi gemido.
“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
3 ¡Quién diese que le conociese, y le hallase! yo iría hasta su trono.
Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
4 Ordenaría juicio delante de él, y mi boca henchiría de argumentos.
Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
5 Yo sabría lo que él me respondería, y entendería lo que me dijese.
Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
6 ¿Pleitearía conmigo con multitud de fuerza? No: antes él la pondría en mí.
Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
7 Allí el recto disputaría con él; y escaparía para siempre de él que me condena.
Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
8 He aquí, yo iré al oriente, y no le hallaré, y al occidente, y no le entenderé.
“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
9 Si al norte él obrare, yo no le veré: al mediodía se esconderá, y no le veré.
Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
10 Mas él conoció mi camino: probóme, y salí como oro.
Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
11 Mis pies tomaron su rastro: guardé su camino, y no me aparté.
Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
12 Del mandamiento de sus labios nunca me quité: las palabras de su boca guardé más que mi comida.
Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
13 Y si él se determina en una cosa, ¿quién le apartará? Su alma deseó, e hizo.
“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
14 Por tanto él acabará lo que ha determinado de mí; y muchas cosas como estas hay en él.
Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
15 Por lo cual yo me espantaré delante de su rostro: consideraré, y temerle he.
Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
16 Dios ha enternecido mi corazón, y el Omnipotente me ha espantado.
Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
17 ¿Por qué yo no fui cortado delante de las tinieblas, y cubrió con oscuridad mi rostro?
Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

< Job 23 >