< Job 12 >

1 Y respondió Job, y dijo:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Ciertamente que vosotros sois el pueblo, y con vosotros morirá la sabiduría.
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 También tengo yo seso como vosotros: no soy yo menos que vosotros; ¿y quién habrá que no pueda decir otro tanto?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 El que invoca a Dios, y él le responde, es burlado de su amigo; y el justo y perfecto es escarnecido.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 La antorcha es tenida en poco en el pensamiento del próspero: la cual se aparejó contra las caídas de los pies.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Las tiendas de los robadores están en paz; y los que provocan a Dios, y los que traen dioses en sus manos, viven seguros.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Mas ciertamente pregunta ahora a las bestias, que ellas te enseñarán; y a las aves de los cielos, que ellas te mostrarán:
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 O habla a la tierra, que ella te enseñará; y los peces de la mar te declararán.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 ¿Qué cosa de todas estas no entiende que la mano de Jehová la hizo,
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 Y que en su mano está el alma de todo viviente, el espíritu de toda carne humana?
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Ciertamente el oído prueba las palabras, y el paladar gusta las viandas.
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 En los viejos está la ciencia, y en longura de días la inteligencia.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 Con el está la sabiduría y la fortaleza, suyo es el consejo y la inteligencia.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 He aquí, el derribará, y no será edificado: encerrará al hombre, y no habrá quien le abra.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 He aquí, él detendrá las aguas, y se secarán: él las enviará, y destruirán la tierra.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Con él está la fortaleza y la existencia: suyo es el que yerra, y el que hace errar.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 El hace andar a los consejeros desnudos, y hace enloquecer a los jueces.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 El suelta la atadura de los tiranos, y les ata la cinta en sus lomos.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 El lleva despojados a los príncipes, y él trastorna a los valientes.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 El quita la habla a los que dicen verdad, y el toma el consejo a los ancianos.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 El derrama menosprecio sobre los príncipes, y enflaquece la fuerza de los esforzados.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 El descubre las profundidades de las tinieblas, y saca a luz la sombra de muerte.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 El multiplica las gentes, y él las pierde: él esparce las gentes, y las torna a recoger.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 El quita el seso de las cabezas del pueblo de la tierra, y los hace que se pierdan vagueando sin camino:
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 Que palpen las tinieblas, y no la luz: y los hace errar como borrachos.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< Job 12 >