< Salmos 121 >
1 Levantaré mis ojos a las montañas. ¿De dónde vendrá mi socorro?
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Mi socorro [viene] de Yavé, Quien hizo [el] cielo y [la] tierra.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 No permitirá que tu pie resbale, Ni se dormirá el que te guarda.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 Ciertamente, no se adormecerá ni dormirá, El que guarda a Israel.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 Yavé es tu Guardador, Yavé es tu Sombra a tu mano derecha.
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 El sol no te fatigará de día, Ni la luna de noche.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 Yavé te protegerá de todo mal. Él guardará tu alma.
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 Yavé guardará tu salida y tu entrada Desde ahora y para siempre.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.