< Salmos 112 >

1 ¡Aleluya! Inmensamente feliz es el hombre que teme a Yavé, Que grandemente se deleita en sus Mandamientos.
Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 Sus descendientes serán poderosos en la tierra. La generación de los rectos será bendita.
Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3 Suficiencia y riquezas hay en su casa, Y su justicia permanece para siempre.
Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Luz resplandece en las tinieblas para el recto. Es bondadoso, compasivo y justo.
Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5 Anda bien el hombre que es bondadoso y presta. Mantendrá su causa en el juicio.
Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6 Porque él nunca será conmovido, El justo será recordado para siempre.
Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7 No tendrá temor de malas noticias. Su corazón está firme, confiado en Yavé.
Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8 Su corazón está sostenido. No temerá hasta que mire desde arriba a sus adversarios.
Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9 El reparte libremente a los pobres. Su justicia permanece para siempre. Su poder es exaltado con honor.
Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10 Lo verá el perverso y se angustiará. Crujirá sus dientes y se consumirá. El deseo de los perversos perecerá.
Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.

< Salmos 112 >