< Proverbios 15 >

1 La amable respuesta aplaca la ira, Pero la palabra hiriente aumenta el furor.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 La lengua de los sabios hace aceptable el conocimiento, La boca de los necios expresa insensatez.
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 Los ojos de Yavé están en todo lugar, Y observan a malos y a buenos.
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 Árbol de vida es la boca apacible, Pero la perversa es quebrantamiento de espíritu.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 El necio desprecia el consejo de su padre, Pero el que acepta la corrección es sagaz.
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 En la casa del justo hay gran riqueza, Pero en las ganancias del perverso hay aflicción.
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 Los labios de los sabios esparcen conocimiento, No así el corazón de los necios.
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 Repugnancia a Yavé es el sacrificio de los perversos, Pero la oración de los rectos es su deleite.
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 Repugnancia a Yavé es el camino del perverso, Pero Él ama al que sigue la justicia.
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 La disciplina molesta al que abandona el camino. El que aborrece la corrección morirá.
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 El Seol y el Abadón están delante de Yavé, ¡Cuánto más los corazones de los hijos de hombres! (Sheol h7585)
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol h7585)
12 El escarnecedor no ama al que lo reprende, Ni busca a los sabios.
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 Un corazón alegre hermosea el rostro, Pero el dolor del corazón abate el ánimo.
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 El corazón entendido busca el conocimiento, Pero la boca de los necios se apacienta de la insensatez.
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 Todos los días del afligido son difíciles, Pero el de corazón alegre [tiene] un banquete continuo.
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 Más vale poco con el temor a Yavé, Que grandes tesoros con tumulto.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Mejor es ración de legumbres donde hay amor, Que buey engordado donde hay rencor.
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 El hombre iracundo provoca contiendas, Pero el lento para la ira apacigua la rencilla.
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 El camino del perezoso es como un cercado de espinos, Pero la senda de los rectos es llana.
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 El hijo sabio alegra al padre, Pero el hombre necio menosprecia a su madre.
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 La necedad divierte al falto de entendimiento, Pero el hombre prudente endereza su andar.
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 Sin consulta, los planes se frustran, Pero tienen éxito con muchos consejeros.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 El hombre se alegra con la respuesta de su boca. ¡Cuán buena es la palabra oportuna!
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 El prudente sube por el camino de la vida, Que lo aparta de la bajada al Seol. (Sheol h7585)
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol h7585)
25 Yavé destruye la casa del soberbio, Pero afirma el lindero de la viuda.
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 Repugnancia a Yavé son los pensamientos del perverso, Pero las palabras de los puros le son placenteras.
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 El que aspira a ganancias deshonestas arruina su casa, Pero el que aborrece el soborno vivirá.
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 El corazón del justo medita la respuesta, Pero la boca del perverso derrama malas cosas.
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 Yavé está lejos de los perversos, Pero escucha la oración de los justos.
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 La luz de los ojos alegra el corazón, Y una buena noticia nutre los huesos.
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 Oído que escucha sana reprensión, Vivirá entre los sabios.
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 El que rechaza la corrección menosprecia su vida, El que escucha la amonestación adquiere entendimiento.
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 El temor a Yavé es escuela de sabiduría, Y antes del honor está la humildad.
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.

< Proverbios 15 >