< Proverbios 14 >
1 La mujer sabia edifica su casa, La necia con sus manos la derriba.
Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
2 El que anda en su rectitud teme a Yavé, Pero el de caminos torcidos lo desprecia.
Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
3 En la boca del necio hay una vara para su espalda, Pero los sabios son protegidos por sus labios.
Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
4 Donde no hay bueyes el establo está limpio, Pero mucho rendimiento hay por la fuerza del buey.
Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
5 El testigo veraz no miente, Pero el testigo falso respira mentiras.
Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
6 El burlador busca la sabiduría y no la halla, Pero el conocimiento es fácil para el que tiene entendimiento.
Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
7 Apártate de la presencia del necio, Porque en él no hallarás palabras de conocimiento.
Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
8 Entender el camino es sabiduría del sagaz, Pero la necedad de los necios es engaño.
Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
9 Se burla el necio del pecado, Pero entre los rectos hay buena voluntad.
Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
10 El corazón conoce su propia amargura, Y en su alegría no participa el extraño.
Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
11 La casa de los perversos será asolada, Pero la morada de los rectos florecerá.
Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
12 Hay camino que al hombre parece derecho, Pero su fin es camino de muerte.
Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
13 Aun entre risas llora el corazón, Y el final de la alegría es tristeza.
Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
14 El insensato se hartará de sus propios caminos, Pero el hombre bueno estará satisfecho con el suyo.
Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
15 El ingenuo cree cualquier cosa, Pero el prudente considera sus pasos.
Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
16 El sabio teme y se aparta del mal, Pero el necio se lanza confiado.
Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
17 El que fácilmente se aíra hará locuras, Y el hombre perverso será aborrecido.
Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
18 Los ingenuos heredan insensatez, Pero el prudente se corona de conocimiento.
Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
19 Los perversos se inclinarán ante los buenos, Y los perversos ante las puertas del justo.
Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
20 El pobre es odiado aun por su vecino, Pero muchos son los que aman al rico.
Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
21 El que menosprecia a su prójimo peca, Pero el que se compadece de los pobres es inmensamente feliz.
Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
22 ¿No yerran los que piensan mal? Pero misericordia y verdad son para los que piensan el bien.
Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
23 En toda labor hay fruto, Pero la palabra solo de labios lleva a la indigencia.
Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
24 Corona de los sabios es su riqueza, Pero la insensatez de los necios es locura.
Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
25 Un testigo veraz salva vidas, Pero el engañador habla mentiras.
Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
26 En el temor a Yavé hay fuerte confianza Que servirá de refugio a los hijos.
Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
27 El temor a Yavé es manantial de vida, Que aparta de las trampas de la muerte.
Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
28 En la multitud de pueblo está la gloria del rey, Y en la falta de pueblo la flaqueza del gobernante.
Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
29 El que tarda en airarse tiene gran entendimiento, Pero el impulsivo exalta la necedad.
Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
30 Un corazón tranquilo es vida para el cuerpo, Pero la envidia es carcoma en los huesos.
Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
31 El que oprime al pobre afrenta a su Hacedor, Pero lo honra el que favorece al necesitado.
Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
32 Por su propia maldad será derribado el perverso, Pero el justo tiene refugio en su muerte.
Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
33 En el corazón del que tiene entendimiento reposa la sabiduría, Aun en medio de necios se da a conocer.
Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
34 La justicia enaltece a una nación, Pero el pecado es afrenta para los pueblos.
Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
35 La benevolencia del rey es para el esclavo prudente, Pero su enojo contra el que lo avergüenza.
Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.