< Josué 19 >

1 La segunda suerte tocó a la tribu de los hijos de Simeón según sus familias. Su herencia estaba en medio de la heredad de los hijos de Judá.
Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
2 En su heredad tenían Beerseba, Seba, Molada,
Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
3 Hasar-sual, Bala, Esem,
Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
4 Heltolad, Betul, Horma,
Elitoladi, Betuli, Horima,
5 Siclag, Bet-marcabot, Hasar-susa,
Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
6 Bet-lebaot y Saruhén: 13 ciudades con sus aldeas.
Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
7 Y Aín, Rimón, Eter y Asán: cuatro ciudades con sus aldeas.
Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
8 Todas las aldeas que estaban alrededor de estas ciudades hasta Balat-beer, que es Ramat del Neguev. Esta es la heredad de la tribu de los hijos de Simeón, según sus familias.
Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
9 De la porción de los hijos de Judá se tomó la heredad de los hijos de Simeón, ya que la parte de los hijos de Judá era muy grande para ellos. Así que los hijos de Simeón tuvieron su heredad en medio de la herencia de aquéllos.
Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
10 La tercera suerte tocó a los hijos de Zabulón, según sus familias, y el límite de su heredad llegaba hasta Sarid.
Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
11 Por el oeste su límite subía hasta Marala y llegaba hasta Dabeset, y de allí hasta el arroyo que está delante de Jocneam,
Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
12 de Sarid volvía hacia el este, hacia donde sale el sol, hasta el lindero de Quislot-tabor, salía a Daberat y subía a Jafía.
Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
13 De allí pasaba al este, a Gat-jefer, hasta Et-cazín, y se extendía hasta Rimón, la cual limita con Nea.
Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
14 Después el límite giraba al norte, hacia Hanatón, e iba a salir al valle de Jefte-el,
Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
15 donde están Catat, Nahalal, Simrón, Ideala y Belén: 12 ciudades con sus aldeas.
Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
16 Esta es la heredad de los hijos de Zabulón según sus familias. Estas ciudades con sus aldeas.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
17 La cuarta suerte salió para Isacar, para los hijos de Isacar según sus familias.
Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
18 Su territorio fue Jezreel, Quesulot, Sunem,
Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
19 Hafaráim, Sihón, Anaharat,
Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
20 Rabit, Quisión, Ebes,
Rabiti, Kisoni, Ebezi,
21 Remet, En-ganim, En-hada y Bet-pases.
Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
22 El límite llegaba hasta Tabor, Sahasima y Bet-semes, y su lindero terminaba en el Jordán: 16 ciudades con sus aldeas.
Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
23 Esta es la herencia de la tribu de los hijos de Isacar según sus familias. Esas ciudades con sus aldeas.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
24 La quinta suerte salió para la tribu de los hijos de Aser, según sus familias.
Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
25 Su territorio fue: Helcat, Halí, Betén, Acsaf,
Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
26 Alamelec, Amad y Miseal, y llegaba hasta el oeste de la montaña Carmelo y a Sihor-libnat.
Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
27 Después volvía hacia donde sale el sol hasta Bet-dagón, llegaba hasta Zabulón y al valle de Jefte-el, hacia el norte de Bet-emec y a Neiel, y salía por el norte a Cabul,
Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
28 a Hebrón, a Rehob, a Hamón y a Caná, hasta la gran Sidón.
Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
29 De allí el límite volvía hacia Ramá y hacia la ciudad fortificada de Tiro, regresaba hacia Hosa, y salía al mar por el territorio de Aczib,
Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
30 Uma, Afec y Rehob: 22 ciudades con sus aldeas.
Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
31 Esta es la herencia de la tribu de los hijos de Aser según sus familias. Esas ciudades con sus aldeas.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
32 La sexta suerte tocó a los hijos de Neftalí según sus familias.
Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
33 Su lindero iba desde Hélef, Alón-saananim, Adami-néqueb y Jabneel, hasta Lacum, y salía al Jordán.
Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
34 Desde allí el límite volvía hacia el oeste hasta Aznot-tabor, y de allí a Hucoc, y llegaba hasta Zabulón por el sur, y por el oeste limitaba con Aser y con Judá en el Jordán, hacia donde sale sol.
Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
35 Y las ciudades fortificadas eran: Sidim, Ser, Hamat, Racat, Cineret,
Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
36 Adama, Ramá, Hazor,
Adama, Rama, Hazori,
37 Cedes, Edrei, En-hazor,
Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
38 Irón, Migdal-el, Horem, Bet-anat y Bet-semes: 19 ciudades con sus aldeas.
Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
39 Esta es la heredad de la tribu de los hijos de Neftalí según sus familias. Esas ciudades con sus aldeas.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
40 La séptima suerte salió para la tribu de los hijos de Dan por sus familias.
Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
41 El territorio de su herencia fue Zora, Estaol, Ir-semes,
Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
42 Saalabín, Ajalón, Jetla,
Saalabini, Ayaloni, Itira,
43 Elón, Timnat, Ecrón,
Eloni, Timna, Ekroni,
44 Elteque, Gibetón, Baalat,
Eliteke, Gibetoni, Baalati,
45 Jehúd, Bene-berac, Gat-rimón,
Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
46 Me-harcón, y Racón, con el territorio que está frente a Jope.
Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
47 El territorio de los hijos de Dan se amplió, pues subieron y atacaron a Lesem. La capturaron, la pasaron a filo de espada, la poseyeron y se establecieron en ella. A Lesem la llamaron Dan, por el nombre de su antepasado Dan.
Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
48 Esta es la heredad de la tribu de los hijos de Dan según sus familias, esas ciudades con sus aldeas.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
49 Cuando acabaron de distribuir la tierra según sus límites, los hijos de Israel dieron heredad a Josué, hijo de Nun, en medio de ellos.
Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
50 Según el mandamiento de Yavé, le dieron la ciudad que él pidió: Timnat-sera, en la región montañosa de Efraín. Él reedificó la ciudad y vivió en ella.
Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
51 Estas son las heredades que el sacerdote Eleazar y Josué, hijo de Nun, y los jefes de las casas paternas repartieron por sorteo entre las tribus de los hijos de Israel en Silo, en presencia de Yavé, en la entrada del Tabernáculo de Reunión. Así acabaron de repartir la tierra.
Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.

< Josué 19 >