< Job 29 >

1 Entonces Job respondió:
Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Ojalá volviera a ser como en meses pasados, como en los días cuando ʼElohim me vigilaba,
“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
3 cuando su lámpara estaba sobre mi cabeza y a su luz yo caminaba en la oscuridad,
pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
4 aquellos días de mi vigor cuando la amistad íntima de ʼElohim velaba sobre mi vivienda,
Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
5 cuando ʼEL-Shadday aún estaba conmigo, y mis hijos alrededor de mí,
nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
6 cuando mis pasos eran lavados con mantequilla y la roca me derramaba ríos de aceite,
pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
7 cuando iba a la puerta de la ciudad y en la plaza preparaba mi asiento.
“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
8 Los jóvenes me veían y se escondían. Los ancianos se levantaban y permanecían en pie.
anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
9 Los magistrados detenían sus palabras y ponían la mano sobre sus bocas.
atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
10 La voz de los nobles enmudecía y su lengua se les pegaba al paladar.
anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
11 Los oídos que me escuchaban me llamaban bienaventurado, y los ojos que me miraban daban testimonio a mi favor.
Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
12 Porque yo libraba al pobre que clamaba y al huérfano que no tenía ayudador.
chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
13 La bendición del que iba a perecer caía sobre mí, y daba alegría al corazón de la viuda.
Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
14 Me vestía de rectitud y con ella me cubría. Mi justicia era como un manto y un turbante.
Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
15 Yo era ojos para el ciego y pies para el cojo.
Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
16 Era padre de los menesterosos. Me informaba con diligencia de la causa que no entendía.
Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
17 Rompía las quijadas del perverso y de sus dientes arrancaba la presa.
Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
18 Me decía: En mi nido moriré, y como la arena multiplicaré mis días.
“Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
19 Mi raíz se extendía hacia las aguas, y el rocío pernoctaba en mi ramaje.
Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
20 Mi honra se renovaba en mí, y mi arco se fortalecía en mi mano.
Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
21 Me escuchaban, esperaban y guardaban silencio ante mi consejo.
“Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
22 Después de mi palabra no replicaban. Mi razón destilaba sobre ellos.
Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
23 La esperaban como a la lluvia temprana, y abrían su boca como a la lluvia tardía.
Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
24 Si me reía con ellos, no lo creían, y no tenían en menos la luz de mi semblante.
Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
25 Yo les escogía el camino, y me sentaba entre ellos como su jefe. Yo vivía como un rey en medio de su tropa, como el que consuela a los que están de duelo.
Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”

< Job 29 >