< Éxodo 35 >
1 Moisés convocó a toda la congregación de los hijos de Israel y les dijo: Estas son las cosas que Yavé ordenó para que se hagan:
Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
2 Seis días se trabajará, pero el séptimo día será sagrado, sábado de completo reposo para Yavé. Cualquiera que haga alguna obra en él morirá.
Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
3 No encenderán fuego en ninguna de sus tiendas el día sábado.
Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
4 Moisés habló a toda la congregación de los hijos de Israel: Esto es lo que Yavé ordenó:
Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
5 Recojan entre ustedes una ofrenda para Yavé. Todo aquel de corazón generoso llevará la ofrenda para Yavé: oro, plata y bronce,
Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
6 [tela] azul, púrpura y carmesí, lino fino y pelo de cabras,
nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
7 pieles de carnero teñidas de rojo, pieles de tejones y madera de acacia,
zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
8 aceite para el alumbrado, especias aromáticas para el aceite de la unción y para el incienso aromático,
mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
9 y piedras de ónice, piedras de engaste para el efod y para el pectoral.
miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
10 De entre ustedes, todo hábil artesano vendrá y hará todas las cosas que Yavé ordenó:
“Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
11 El Tabernáculo, su tienda y su cubierta, broches, tablones, travesaños, columnas y basas,
Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
12 el Arca y sus varas, el Propiciatorio y el velo que servirá de cortina,
Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
13 la mesa, sus varas y todos sus utensilios, y el Pan de la Presencia,
tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
14 el candelabro para la iluminación, sus utensilios, lámparas y el aceite para la iluminación,
choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
15 el altar del incienso y sus varas, el aceite de la unción y el incienso aromático, la cortina de la puerta para la entrada al Tabernáculo,
guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
16 el altar del holocausto y su rejilla de bronce, varas y todos sus utensilios, la fuente con su basa,
guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
17 las cortinas del patio con sus columnas y sus basas, y la cortina de la entrada al patio,
nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
18 las estacas del Tabernáculo, las estacas del patio y sus cuerdas,
zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
19 las ropas tejidas para ministrar en el Lugar Santo, las ropas sagradas para el sacerdote Aarón, y las ropas de sus hijos para ministrar como sacerdotes.
zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
20 Entonces toda la congregación de los hijos de Israel salió de la presencia de Moisés.
Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
21 Todo aquel a quien su corazón impulsaba y todo aquel a quien movía su espíritu, iba a llevar la ofrenda a Yavé para la obra del Tabernáculo de Reunión, para todo su servicio y para las ropas santas.
ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
22 Acudieron los hombres y las mujeres, todos los de corazón generoso, y llevaron aretes, zarcillos, sortijas, collares, toda clase de joyas de oro, y también todo aquel que había mecido una ofrenda de oro para Yavé.
Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
23 Todo hombre que poseía [tela] azul, púrpura o carmesí, o lino fino, o pelo de cabras, o pieles de carneros pintadas de rojo, o pieles de tejones, llevaba.
Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
24 Todo el que podía dar una contribución de plata o de bronce, llevaba la contribución a Yavé. Todo el que poseía madera de acacia para cualquier obra del servicio, la llevaba.
Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
25 Además, toda mujer sabia hilaba con sus manos y llevaba hilado azul, púrpura y carmesí, y cordoncillo de lino fino.
Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
26 Todas las mujeres cuyo corazón las impulsó con sabiduría, tejieron pelo de cabra.
Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
27 Los jefes aportaron piedras de ónice y de engaste para el efod y el pectoral,
Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
28 las especias, y el aceite para la iluminación, el de la unción y el incienso aromático.
Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
29 Todos los hombres y las mujeres de los hijos de Israel cuyo corazón los impulsó a contribuir en toda la obra que Yavé ordenó hacer por medio de Moisés, llevaron contribución voluntaria a Yavé.
Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
30 Y Moisés dijo a los hijos de Israel: Miren, Yavé llamó por nombre a Bezaleel, hijo de Uri, hijo de Hur, de la tribu de Judá.
Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
31 Lo llenó del Espíritu de ʼElohim en sabiduría, entendimiento, ciencia y en toda clase de obra
ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
32 para hacer diseños, labrar en oro, plata y bronce,
Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
33 en talla de piedras para engastes, para obra de madera y para trabajar en toda labor ingeniosa.
kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
34 También dotó su corazón para enseñar, tanto él como Oholiab, hijo de Ahisamac, de la tribu de Dan,
Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
35 a quienes llenó de sabiduría de corazón para que hagan toda obra de artesanía, de diseño, de bordado en [tela ] azul, púrpura y carmesí y en cordoncillo de lino fino, y de tejedor, para que realicen toda labor y hagan diseños.
Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.