< Sofonías 1 >

1 Palabra de Yahvé que llegó a Sofonías, hijo de Cushi, hijo de Gedalías, hijo de Amarías, hijo de Ezequías, en los días de Josías, hijo de Amón, rey de Judá.
Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
2 Barreré todo de la superficie de la tierra, dice el Señor.
“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
3 Barreré al hombre y al animal. Barreré las aves del cielo, los peces del mar y los montones de escombros con los malvados. Eliminaré al hombre de la superficie de la tierra, dice el Señor.
“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
4 Extenderé mi mano contra Judá y contra todos los habitantes de Jerusalén. Cortaré de este lugar el remanente de Baal, el nombre de los sacerdotes idólatras y paganos,
Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
5 los que adoran al ejército del cielo en las azoteas, los que adoran y juran por Yahvé y también juran por Malcam,
amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
6 los que se han apartado de seguir a Yahvé, y los que no han buscado a Yahvé ni han preguntado por él.
amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
7 Guarda silencio ante la presencia del Señor Yahvé, porque el día de Yahvé está cerca. Porque Yahvé ha preparado un sacrificio. Ha consagrado a sus invitados.
Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
8 El día del sacrificio de Yahvé castigaré a los príncipes, a los hijos del rey y a todos los que se visten con ropas extranjeras.
Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
9 Ese día castigaré a todos los que saltan el umbral, que llenan la casa de su amo con violencia y engaño.
Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
10 En aquel día, dice el Señor, habrá ruido de gritos desde la puerta de los peces, un lamento desde el segundo barrio y un gran estruendo desde las colinas.
“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
11 ¡Llorad, habitantes de Majtés, porque todo el pueblo de Canaán está deshecho! Todos los que estaban cargados de plata han sido eliminados.
Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
12 Sucederá en aquel tiempo que registraré a Jerusalén con lámparas, y castigaré a los hombres asentados en sus escorias, que dicen en su corazón: “Yahvé no hará el bien, ni hará el mal.”
Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
13 Sus riquezas se convertirán en un despojo, y sus casas en una desolación. Sí, construirán casas, pero no las habrán habitado. Plantarán viñas, pero no beberán su vino.
Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
14 El gran día de Yahvé está cerca. Está cerca y se apresura mucho, la voz del día de Yahvé. El poderoso llora allí amargamente.
Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
15 Ese día es un día de ira, un día de angustia y de aflicción, un día de problemas y de ruina, un día de oscuridad y de tinieblas, un día de nubes y de negrura,
Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
16 un día de trompeta y de alarma contra las ciudades fortificadas y contra las altas almenas.
Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
17 Traeré tal angustia sobre los hombres que andarán como ciegos por haber pecado contra Yahvé. Su sangre será derramada como polvo y su carne como estiércol.
Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
18 Ni su plata ni su oro podrán librarlos en el día de la ira de Yahvé, sino que toda la tierra será devorada por el fuego de su celo; porque él acabará, sí, terriblemente, con todos los que habitan la tierra.
Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.

< Sofonías 1 >