< Salmos 85 >

1 Para el músico principal. Un salmo de los hijos de Coré. Yahvé, has sido favorable a tu tierra. Has restaurado la fortuna de Jacob.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 Has perdonado la iniquidad de tu pueblo. Tú has cubierto todo su pecado. (Selah)
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 Has quitado toda tu ira. Te has apartado de la ferocidad de tu ira.
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 Vuélvenos, Dios de nuestra salvación, y haz que cese tu indignación hacia nosotros.
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 ¿Estarás enojado con nosotros para siempre? ¿Sacará su ira a todas las generaciones?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 No nos revivirás de nuevo, para que tu pueblo se regocije en ti?
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Muéstranos tu amorosa bondad, Yahvé. Concédenos tu salvación.
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 Oiré lo que Dios, Yahvé, diga, porque hablará de paz a su pueblo, a sus santos; pero que no vuelvan a la locura.
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Ciertamente su salvación está cerca de los que le temen, para que la gloria habite en nuestra tierra.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 La misericordia y la verdad se unen. La justicia y la paz se han besado.
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 La verdad brota de la tierra. La justicia ha mirado desde el cielo.
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Sí, Yahvé dará lo que es bueno. Nuestra tierra dará sus frutos.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 La justicia va delante deél, y prepara el camino para sus pasos.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.

< Salmos 85 >