< Salmos 81 >
1 Para el músico principal. En un instrumento de Gath. Por Asaf. ¡Canta en voz alta a Dios, nuestra fuerza! ¡Haz un grito de júbilo al Dios de Jacob!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
2 Eleva una canción, y trae aquí la pandereta, la agradable lira con el arpa.
Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
3 Toca la trompeta en la Luna Nueva, en la luna llena, en nuestro día de fiesta.
Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
4 Porque es un estatuto para Israel, una ordenanza del Dios de Jacob.
ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
5 Lo designó en José para un pacto, cuando salió sobre la tierra de Egipto, Oí un idioma que no conocía.
Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
6 “Quité su hombro de la carga. Sus manos se liberaron de la cesta.
Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
7 Llamaste a la angustia, y te libré. Te respondí en el lugar secreto del trueno. Te probé en las aguas de Meribah”. (Selah)
Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
8 “Oíd, pueblo mío, y yo os daré testimonio, ¡Israel, si me escuchas!
“Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
9 No habrá en ti ningún dios extraño, ni adorarás a ningún dios extranjero.
Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
10 Yo soy Yahvé, tu Dios, que te sacó de la tierra de Egipto. Abre bien tu boca y la llenaré.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
11 Pero mi pueblo no escuchó mi voz. Israel no deseaba nada de mí.
“Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
12 Así que los dejé ir tras la terquedad de sus corazones, para que puedan caminar en sus propios consejos.
Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
13 Oh, que mi pueblo me escuche, para que Israel siga mis caminos.
“Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
14 Pronto sometería a sus enemigos, y volver mi mano contra sus adversarios.
nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
15 Los que odian a Yahvé se acobardan ante él, y su castigo duraría para siempre.
Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
16 Pero también los habría alimentado con lo más fino del trigo. Te saciaré con miel de la roca”.
Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”