< Salmos 61 >
1 Para el músico jefe. Para un instrumento de cuerda. Por David. Escucha mi clamor, Dios. Escucha mi oración.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
2 Desde el fin de la tierra, te llamaré cuando mi corazón esté abrumado. Condúceme a la roca que es más alta que yo.
Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
3 Porque tú has sido un refugio para mí, una torre fuerte del enemigo.
Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
4 Yo habitaré en tu tienda para siempre. Me refugiaré al abrigo de tus alas. (Selah)
Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
5 Porque tú, Dios, has escuchado mis votos. Me has dado la herencia de los que temen tu nombre.
Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
6 Prolongarás la vida del rey. Sus años serán para generaciones.
Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
7 Será entronizado en la presencia de Dios para siempre. Designa tu amorosa bondad y la verdad, para que lo preserven.
Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
8 Así cantaré alabanzas a tu nombre para siempre, para que pueda cumplir mis votos diariamente.
Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.