< Salmos 57 >

1 Para el músico jefe. Con la melodía de “No destruyas”. Un poema de David, cuando huyó de Saúl, en la cueva. Ten piedad de mí, Dios, ten piedad de mí, porque mi alma se refugia en ti. Sí, a la sombra de tus alas me refugiaré, hasta que el desastre haya pasado.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
2 Clamo al Dios Altísimo, a Dios que cumple mis peticiones por mí.
Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
3 Él enviará desde el cielo y me salvará, reprende al que me persigue. (Selah) Dios enviará su amorosa bondad y su verdad.
Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
4 Mi alma está entre leones. Me encuentro entre los que se prenden fuego, incluso los hijos de los hombres, cuyos dientes son lanzas y flechas, y su lengua una espada afilada.
Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
5 ¡Sé exaltado, Dios, por encima de los cielos! ¡Que tu gloria esté por encima de toda la tierra!
Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
6 Han preparado una red para mis pasos. Mi alma se inclina. Cavan una fosa antes que yo. Ellos mismos caen en el medio. (Selah)
Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
7 Mi corazón está firme, Dios. Mi corazón es firme. Cantaré, sí, cantaré alabanzas.
Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
8 ¡Despierta, mi gloria! ¡Despierta, laúd y arpa! Despertaré al amanecer.
Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
9 Te daré gracias, Señor, entre los pueblos. Te cantaré alabanzas entre las naciones.
Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
10 Porque tu gran bondad llega hasta los cielos, y tu verdad a los cielos.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
11 Sé exaltado, Dios, por encima de los cielos. Que tu gloria sea sobre toda la tierra.
Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

< Salmos 57 >