< Salmos 48 >
1 Una canción. Un salmo de los hijos de Coré. Grande es Yahvé, y digno de gran alabanza, en la ciudad de nuestro Dios, en su santo monte.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 Hermoso en elevación, la alegría de toda la tierra, es el Monte Zion, en los lados norte, la ciudad del gran Rey.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 Dios se ha mostrado en sus ciudadelas como un refugio.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 Pues he aquí que los reyes se han reunido, pasaron juntos.
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 Lo vieron y se asombraron. Estaban consternados. Se apresuraron a marcharse.
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 El temblor se apoderó de ellos allí, dolor, como el de una mujer de parto.
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 Con el viento del este, rompes las naves de Tarsis.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 Como hemos oído, hemos visto, en la ciudad de Yahvé de los Ejércitos, en la ciudad de nuestro Dios. Dios lo establecerá para siempre. (Selah)
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 Hemos pensado en tu amorosa bondad, Dios, en el centro de su templo.
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 Como tu nombre, Dios, así es tu alabanza hasta los confines de la tierra. Tu mano derecha está llena de justicia.
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 ¡Que se alegre el monte Sión! Que las hijas de Judá se alegren por tus juicios.
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 Camina alrededor de Sión y rodéala. Numerar sus torres.
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 Fíjate en sus baluartes. Considera sus palacios, para que lo cuentes a la siguiente generación.
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 Porque este Dios es nuestro Dios por los siglos de los siglos. Él será nuestro guía incluso hasta la muerte.
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.