< Salmos 42 >

1 Para el músico principal. Una contemplación de los hijos de Coré. Como el ciervo que busca los arroyos de agua, por lo que mi alma suspira por ti, Dios.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi, kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.
2 Mi alma tiene sed de Dios, del Dios vivo. ¿Cuándo vendré a comparecer ante Dios?
Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo. Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?
3 Mis lágrimas han sido mi alimento día y noche, mientras me preguntan continuamente: “¿Dónde está tu Dios?”
Misozi yanga yakhala chakudya changa usana ndi usiku, pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
4 De esto me acuerdo, y derramo mi alma dentro de mí, cómo solía ir con la multitud, y los llevaba a la casa de Dios, con voz de alegría y alabanza, una multitud que celebra un día santo.
Zinthu izi ndimazikumbukira pamene ndikukhuthula moyo wanga: momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu, kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko pakati pa anthu a pa chikondwerero.
5 ¿Por qué te desesperas, alma mía? ¿Por qué te perturbas dentro de mí? ¡Espera en Dios! Porque aún le alabaré por la ayuda salvadora de su presencia.
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Yembekezera Mulungu, pakuti ndidzamulambirabe, Mpulumutsi wanga ndi
6 Dios mío, mi alma está desesperada dentro de mí. Por eso me acuerdo de ti desde la tierra del Jordán, las alturas del Hermón, desde la colina Mizar.
Mulungu wanga. Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga kotero ndidzakumbukira Inu kuchokera ku dziko la Yorodani, ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.
7 Llamadas profundas al ruido de sus cascadas. Todas tus olas y tus olas me han barrido.
Madzi akuya akuyitana madzi akuya mu mkokomo wa mathithi anu; mafunde anu onse obwera mwamphamvu andimiza.
8 Yahvé ordenará su bondad amorosa durante el día. En la noche su canción estará conmigo: una oración al Dios de mi vida.
Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake, nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane; pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.
9 Preguntaré a Dios, mi roca: “¿Por qué me has olvidado? ¿Por qué voy de luto por la opresión del enemigo?”
Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa, “Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?”
10 Como con una espada en los huesos, mis adversarios me reprochan, mientras me preguntan continuamente: “¿Dónde está tu Dios?”
Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo pamene adani anga akundinyoza, tsiku lonse akunena kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
11 ¿Por quéestás desesperada, alma mía? ¿Por qué te perturbas dentro de mí? ¡Espera en Dios! Porque todavía lo alabaré, la ayuda salvadora de mi rostro, y mi Dios.
Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

< Salmos 42 >