< Salmos 33 >
1 ¡Alégrense en Yahvé, justos! La alabanza es propia de los rectos.
Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
2 Da gracias a Yahvé con la lira. Cántale alabanzas con el arpa de diez cuerdas.
Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
3 Cántale una nueva canción. ¡Juega con habilidad y con un grito de alegría!
Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
4 Porque la palabra de Yahvé es justa. Todo su trabajo se realiza con fidelidad.
Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
5 Ama la rectitud y la justicia. La tierra está llena de la bondad amorosa de Yahvé.
Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
6 Por la palabra de Yahvé se hicieron los cielos: todo su ejército por el aliento de su boca.
Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
7 Reúne las aguas del mar como un montón. Él guarda las profundidades en almacenes.
Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
8 Que toda la tierra tema a Yahvé. Que todos los habitantes del mundo le teman.
Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
9 Porque él habló, y fue hecho. Lo ordenó, y se mantuvo firme.
Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
10 Yahvé hace fracasar el consejo de las naciones. Hace que los pensamientos de los pueblos no tengan efecto.
Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
11 El consejo de Yahvé se mantiene firme para siempre, los pensamientos de su corazón a todas las generaciones.
Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
12 Bendita es la nación cuyo Dios es Yahvé, el pueblo que ha elegido para su propia herencia.
Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 Yahvé mira desde el cielo. Él ve a todos los hijos de los hombres.
Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
14 Desde el lugar de su morada mira a todos los habitantes de la tierra,
kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 el que modela todos sus corazones; y considera todas sus obras.
Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
16 No hay rey que se salve por la multitud de un ejército. Un hombre poderoso no se libra por su gran fuerza.
Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 Un caballo es una cosa vana para la seguridad, ni libera a ninguno por su gran poder.
Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 He aquí que el ojo de Yahvé está sobre los que le temen, a los que esperan en su amorosa bondad,
Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 para librar su alma de la muerte, para mantenerlos vivos en la hambruna.
kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 Nuestra alma ha esperado a Yahvé. Él es nuestra ayuda y nuestro escudo.
Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 Porque nuestro corazón se regocija en él, porque hemos confiado en su santo nombre.
Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 Que tu bondad sea con nosotros, Yahvé, ya que hemos esperado en ti.
Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.