< Salmos 25 >

1 Por David. A ti, Yahvé, elevo mi alma.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 Dios mío, en ti he confiado. No dejes que me avergüence. No dejes que mis enemigos triunfen sobre mí.
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 Sí, nadie que te espere será avergonzado. Serán avergonzados los que traicionen sin causa.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Muéstrame tus caminos, Yahvé. Enséñame tus caminos.
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Guíame en tu verdad y enséñame, porque tú eres el Dios de mi salvación. Te espero todo el día.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Yahvé, acuérdate de tus misericordias y de tu bondad, porque son de los viejos tiempos.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 No te acuerdes de los pecados de mi juventud, ni de mis transgresiones. Acuérdate de mí según tu amorosa bondad, por tu bondad, Yahvé.
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Bueno y recto es Yahvé, por lo que instruirá a los pecadores en el camino.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Él guiará a los humildes en la justicia. Enseñará a los humildes su camino.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Todos los caminos de Yahvé son la bondad y la verdad a los que guardan su pacto y sus testimonios.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Por tu nombre, Yahvé, perdona mi iniquidad, porque es grande.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 ¿Qué hombre es el que teme a Yahvé? Lo instruirá en el camino que elija.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Su alma habitará tranquila. Su descendencia heredará la tierra.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 La amistad de Yahvé está con los que le temen. Él les mostrará su pacto.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Mis ojos están siempre en Yahvé, porque él sacará mis pies de la red.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Vuélvete a mí y ten piedad de mí, porque estoy desolado y afligido.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Los problemas de mi corazón se agrandan. Oh, sácame de mis angustias.
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Considera mi aflicción y mis trabajos. Perdona todos mis pecados.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Considera a mis enemigos, porque son muchos. Me odian con un odio cruel.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Guarda mi alma y líbrame. No permitas que me desilusione, pues me refugio en ti.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Que la integridad y la rectitud me preserven, porque te espero.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Dios, redime a Israel de todos sus problemas.
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Salmos 25 >