< Salmos 15 >

1 Un salmo de David. Yahvé, ¿quién habitará en tu santuario? ¿Quién vivirá en tu santa colina?
Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
2 El que camina intachablemente y hace lo que es correcto, y dice la verdad en su corazón;
Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
3 el que no calumnia con su lengua, ni hace el mal a su amigo, ni lanza calumnias contra sus semejantes;
ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
4 a cuyos ojos se desprecia al hombre vil, sino que honra a los que temen a Yahvé; el que mantiene un juramento aunque le duela, y no cambia;
amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
5 el que no presta su dinero por usura, ni aceptar un soborno contra el inocente. El que hace estas cosas nunca será sacudido.
amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.

< Salmos 15 >