< Salmos 105 >

1 ¡Den gracias a Yahvé! ¡Invoca su nombre! Haz que se conozcan sus actos entre los pueblos.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 ¡Cantadle, cantadle alabanzas! Cuenta todas sus maravillosas obras.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Gloria a su santo nombre. Que se alegre el corazón de los que buscan a Yahvé.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Busca a Yahvé y su fuerza. Busca su rostro para siempre.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Acuérdate de las maravillas que ha hecho: sus maravillas, y los juicios de su boca,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 tú, descendiente de Abraham, su siervo, vosotros, hijos de Jacob, sus elegidos.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Él es Yahvé, nuestro Dios. Sus juicios están en toda la tierra.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Se ha acordado de su pacto para siempre, la palabra que ordenó a mil generaciones,
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 el pacto que hizo con Abraham, su juramento a Isaac,
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 y se lo confirmó a Jacob por un estatuto; a Israel por un pacto eterno,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 diciendo: “A ti te daré la tierra de Canaán, el lote de tu herencia”.
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 cuando no eran más que unos pocos hombres, sí, muy pocos, y extranjeros en ella.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 Iban de nación en nación, de un reino a otro pueblo.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 No permitió que nadie les hiciera mal. Sí, reprendió a los reyes por su bien,
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 “¡No toquen a mis ungidos! No hagas daño a mis profetas”.
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Convocó una hambruna en la tierra. Destruyó los suministros de alimentos.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Envió a un hombre delante de ellos. José fue vendido como esclavo.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 Le magullaron los pies con grilletes. Su cuello fue encerrado con grilletes,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 hasta el momento en que ocurrió su palabra, y la palabra de Yahvé le dio la razón.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 El rey envió y lo liberó, incluso el gobernante de los pueblos, y déjalo libre.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Lo hizo señor de su casa, y gobernante de todas sus posesiones,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 para disciplinar a sus príncipes a su antojo, y para enseñar la sabiduría a sus mayores.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Israel también llegó a Egipto. Jacob vivía en la tierra de Cam.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Aumentó su pueblo en gran medida, y los hizo más fuertes que sus adversarios.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Hizo que su corazón se volviera a odiar a su pueblo, para conspirar contra sus sirvientes.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Envió a Moisés, su siervo, y Aarón, a quienes había elegido.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Hicieron milagros entre ellos, y maravillas en la tierra de Jamón.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Envió las tinieblas y las hizo oscuras. No se rebelaron contra sus palabras.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Convirtió sus aguas en sangre, y mató a sus peces.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Su tierra se llenó de ranas, incluso en las habitaciones de sus reyes.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Habló, y vinieron enjambres de moscas, y piojos en todas sus fronteras.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Les dio granizo como lluvia, con un rayo en su tierra.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 Hirió sus vides y también sus higueras, y destrozaron los árboles de su país.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Él habló, y las langostas vinieron con los saltamontes, sin número.
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 Se comieron todas las plantas de su tierra, y comieron el fruto de su tierra.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 También hirió a todos los primogénitos de su tierra, las primicias de toda su hombría.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Los sacó con plata y oro. No había una sola persona débil entre sus tribus.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Egipto se alegró cuando partieron, porque el miedo a ellos había caído sobre ellos.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Extendió una nube como cobertura, fuego para dar luz en la noche.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 Le pidieron, y trajo codornices, y los satisfizo con el pan del cielo.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Abrió la roca y las aguas brotaron. Corrían como un río en los lugares secos.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 Porque se acordó de su santa palabra, y Abraham, su siervo.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 Sacó a su pueblo con alegría, su elegido con el canto.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 Les dio las tierras de las naciones. Tomaron el trabajo de los pueblos en posesión,
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 para que cumplan sus estatutos, y observar sus leyes. ¡Alabado sea Yah!
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Salmos 105 >