< Proverbios 4 >

1 Escuchad, hijos, la instrucción de un padre. Presta atención y conoce la comprensión;
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 porque te doy un aprendizaje sólido. No abandones mi ley.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Porque yo era hijo de mi padre, tierna y única a los ojos de mi madre.
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 Me enseñó y me dijo: “Que tu corazón retenga mis palabras. Guarda mis mandamientos y vive.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Obtenga sabiduría. Compréndelo. No lo olvides, y no te desvíes de las palabras de mi boca.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 No la abandones, y ella te preservará. Ámala, y ella te mantendrá.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 La sabiduría es suprema. Consigue sabiduría. Sí, aunque te cueste todas tus posesiones, sé comprensivo.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Estimadla, y ella os exaltará. Ella te llevará al honor cuando la abraces.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Ella dará a tu cabeza una guirnalda de gracia. Te entregará una corona de esplendor”.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Escucha, hijo mío, y recibe mis palabras. Los años de tu vida serán muchos.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Te he enseñado el camino de la sabiduría. Te he guiado por caminos rectos.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Cuando vayas, tus pasos no se verán obstaculizados. Cuando corras, no tropezarás.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Agarra firmemente la instrucción. No la dejes ir. Quédate con ella, porque es tu vida.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 No entres en el camino de los malvados. No sigas el camino de los hombres malos.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Evítalo y no pases de largo. Apártate de él y pasa de largo.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Porque no duermen si no hacen el mal. Se les quita el sueño, a menos que hagan caer a alguien.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Porque comen el pan de la maldad y beber el vino de la violencia.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Pero el camino de los justos es como la luz del amanecer que brilla más y más hasta el día perfecto.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 El camino de los malvados es como la oscuridad. No saben con qué tropiezan.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Hijo mío, atiende a mis palabras. Poned el oído en mis palabras.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Que no se aparten de tus ojos. Manténgalos en el centro de su corazón.
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Porque son la vida para los que las encuentran, y salud a todo su cuerpo.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Guarda tu corazón con toda diligencia, porque de ella brota el manantial de la vida.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Aparta de ti la boca perversa. Poner los labios corruptos lejos de ti.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Deja que tus ojos miren al frente. Fija tu mirada directamente delante de ti.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Haz que el camino de tus pies sea llano. Que se establezcan todos sus caminos.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 No te vuelvas a la derecha ni a la izquierda. Retira tu pie del mal.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Proverbios 4 >