< Proverbios 24 >
1 No tengas envidia de los hombres malos, ni el deseo de estar con ellos;
Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
2 para que sus corazones traman la violencia y sus labios hablan de travesuras.
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
3 A través de la sabiduría se construye una casa; mediante la comprensión se establece;
Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
4 por conocimiento las habitaciones se llenan con todos los tesoros raros y hermosos.
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
5 Un hombre sabio tiene un gran poder. Un hombre con conocimientos aumenta la fuerza,
Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
6 pues con una sabia guía libras tu guerra, y la victoria está en muchos asesores.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
7 La sabiduría es demasiado elevada para un tonto. No abre la boca en la puerta.
Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
8 El que conspira para hacer el mal se le llamará intrigante.
Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
9 Los planes de la locura son pecado. El burlador es detestado por los hombres.
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
10 Si flaqueas en el momento de la dificultad, tu fuerza es pequeña.
Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
11 ¡Rescata a los que están siendo llevados a la muerte! En efecto, ¡retened a los que se tambalean hacia la matanza!
Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 Si dices: “He aquí que no sabíamos esto” ¿acaso el que pesa los corazones no lo considera? El que guarda tu alma, ¿no lo sabe? ¿No ha de dar a cada uno según su trabajo?
Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
13 Hijo mío, come miel, porque es buena, los excrementos del panal, que son dulces a su gusto;
Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 así conocerás que la sabiduría es para tu alma. Si lo has encontrado, habrá una recompensa: Su esperanza no será cortada.
Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
15 No aceches, malvado, contra la morada de los justos. No destruyas su lugar de descanso;
Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 porque el justo cae siete veces y se levanta, pero los malvados son derribados por la calamidad.
paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
17 No te alegres cuando tu enemigo caiga. No dejes que tu corazón se alegre cuando sea derrocado,
Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 no sea que Yahvé lo vea y le desagrade, y aleja de él su ira.
Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
19 No te preocupes por los malhechores, ni tengas envidia de los malvados;
Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 porque no habrá recompensa para el hombre malo. La lámpara de los malvados se apagará.
paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
21 Hijo mío, teme a Yahvé y al rey. No te unas a los rebeldes,
Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 porque su calamidad surgirá de repente. ¿Quién sabe qué destrucción puede venir de ambos?
awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
23 Estos son también los dichos de los sabios: Mostrar parcialidad en el juicio no es bueno.
Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 El que dice al impío: “Eres justo” los pueblos lo maldecirán, y las naciones lo aborrecerán —
Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 pero les irá bien a los que condenen a los culpables, y una rica bendición vendrá sobre ellos.
Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
26 Una respuesta sincera es como un beso en los labios.
Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
27 Prepara tu trabajo en el exterior, y preparen sus campos. Después, construye tu casa.
Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
28 No seas testigo contra tu prójimo sin motivo. No engañes con tus labios.
Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 No digas: “Haré con él lo que él ha hecho conmigo”; Pagaré al hombre según su trabajo”.
Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
30 Pasé por el campo del perezoso, por la viña del hombre vacío de entendimiento.
Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 He aquí que todo estaba cubierto de espinas. Su superficie estaba cubierta de ortigas, y su muro de piedra fue derribado.
Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 Entonces vi, y consideré bien. Vi y recibí instrucción:
Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 un poco de sueño, un poco de sopor, un pequeño pliegue de las manos para dormir,
Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 por lo que su pobreza vendrá como un ladrón y su necesidad como hombre armado.
umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.