< Proverbios 14 >

1 Toda mujer sabia construye su casa, pero la insensata lo derriba con sus propias manos.
Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
2 El que camina en su rectitud teme a Yahvé, pero el que es perverso en sus caminos lo desprecia.
Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
3 La palabrería del necio trae una vara a su espalda, pero los labios de los sabios los protegen.
Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
4 Donde no hay bueyes, el pesebre está limpio, pero mucho aumento es por la fuerza del buey.
Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
5 Un testigo veraz no miente, pero un testigo falso vierte mentiras.
Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
6 El burlón busca la sabiduría y no la encuentra, pero el conocimiento llega fácilmente a una persona con criterio.
Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
7 Aléjate de un hombre necio, porque no encontrarás conocimiento en sus labios.
Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
8 La sabiduría del prudente es pensar en su camino, pero la locura de los tontos es el engaño.
Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
9 Los tontos se burlan de la expiación de los pecados, pero entre los rectos hay buena voluntad.
Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
10 El corazón conoce su propia amargura y alegría; no los compartirá con un extraño.
Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
11 La casa de los malvados será derribada, pero la tienda de los rectos florecerá.
Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
12 Hay un camino que le parece correcto al hombre, pero al final lleva a la muerte.
Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
13 Incluso en la risa el corazón puede estar triste, y la alegría puede acabar en pesadez.
Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
14 El infiel será pagado por sus propios caminos; De la misma manera, un buen hombre será recompensado por sus caminos.
Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
15 Un hombre sencillo se lo cree todo, pero el hombre prudente considera cuidadosamente sus caminos.
Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
16 El hombre sabio teme y evita el mal, pero el tonto es un calentón y un imprudente.
Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
17 El que se enoja rápidamente comete una locura, y un hombre astuto es odiado.
Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
18 Los simples heredan la locura, pero los prudentes están coronados por el conocimiento.
Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
19 Los malos se inclinan ante los buenos, y los malvados a las puertas de los justos.
Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
20 El pobre es rechazado incluso por su propio vecino, pero el rico tiene muchos amigos.
Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
21 El que desprecia a su prójimo peca, pero el que se apiada de los pobres es bienaventurado.
Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
22 ¿No se extravían los que traman el mal? Pero el amor y la fidelidad pertenecen a los que planean el bien.
Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
23 En todo trabajo duro hay un beneficio, pero la palabrería de los labios sólo conduce a la pobreza.
Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
24 La corona de los sabios es su riqueza, pero la necedad de los necios los corona de necedad.
Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
25 Un testigo veraz salva almas, pero un testigo falso es engañoso.
Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
26 En el temor de Yahvé hay una fortaleza segura, y será un refugio para sus hijos.
Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
27 El temor de Yahvé es una fuente de vida, apartando a la gente de las trampas de la muerte.
Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
28 En la multitud del pueblo está la gloria del rey, pero en la falta de gente está la destrucción del príncipe.
Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
29 El que es lento para la ira tiene un gran entendimiento, pero el que tiene un temperamento rápido muestra la locura.
Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
30 La vida del cuerpo es un corazón en paz, pero la envidia pudre los huesos.
Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
31 El que oprime a los pobres desprecia a su Hacedor, pero el que es bondadoso con el necesitado lo honra.
Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
32 El impío es abatido en su calamidad, pero en la muerte, el justo tiene un refugio.
Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
33 La sabiduría descansa en el corazón de quien tiene entendimiento, y se da a conocer incluso en el interior de los tontos.
Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
34 La justicia enaltece a una nación, pero el pecado es una desgracia para cualquier pueblo.
Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
35 El favor del rey es para el siervo que trata con sabiduría, pero su ira es hacia el que causa vergüenza.
Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

< Proverbios 14 >