< Proverbios 1 >
1 Los proverbios de Salomón, hijo de David, rey de Israel:
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 para conocer la sabiduría y la instrucción; para discernir las palabras del entendimiento;
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 para recibir instrucción en el trato sabio, en la rectitud, la justicia y la equidad;
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 para dar prudencia a los simples, conocimiento y discreción al joven —
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 para que el sabio escuche y aumente su aprendizaje; para que el hombre de entendimiento alcance el sano consejo;
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 para entender un proverbio y parábolas, las palabras y acertijos de los sabios.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 El temor a Yahvé es el principio del conocimiento, pero los necios desprecian la sabiduría y la instrucción.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Hijo mío, escucha la instrucción de tu padre, y no abandones las enseñanzas de tu madre;
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 pues serán una guirnalda que adornará tu cabeza, y cadenas alrededor del cuello.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Hijo mío, si los pecadores te atraen no lo consienten.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 Si dicen: “Ven con nosotros. Acechemos la sangre. Acechemos en secreto a los inocentes sin causa.
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Que se los trague vivos como el Seol, y entero, como los que bajan a la fosa. (Sheol )
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
13 Encontraremos toda la riqueza valiosa. Llenaremos nuestras casas con el botín.
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Echarán su suerte entre nosotros. Todos tendremos un bolso”—
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 hijo mío, no camines por el camino con ellos. Mantén tu pie fuera de su camino,
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 porque sus pies corren hacia el mal. Se apresuran a derramar sangre.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Porque la red se tiende en vano a la vista de cualquier ave;
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 pero estos acechan su propia sangre. Acechan en secreto por sus propias vidas.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Así son los caminos de todo aquel que tiene afán de lucro. Le quita la vida a sus dueños.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 La sabiduría llama en voz alta en la calle. Ella pronuncia su voz en las plazas públicas.
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 Llama a la cabeza de los lugares ruidosos. A la entrada de las puertas de la ciudad, pronuncia sus palabras:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 “¿Hasta cuándo, simples, amaréis la sencillez? Cuánto tiempo se deleitarán los burladores en la burla, ¿y los tontos odian el conocimiento?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Vuélvete ante mi reprimenda. Mira, derramaré mi espíritu sobre ti. Te daré a conocer mis palabras.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Porque te he llamado y te has negado; He extendido mi mano y nadie me ha hecho caso;
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 pero has ignorado todos mis consejos, y no quería ninguna de mis reprimendas;
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 Yo también me reiré de tu desastre. Me burlaré cuando la calamidad te alcance,
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 cuando la calamidad te alcanza como una tormenta, cuando tu desastre llega como un torbellino, cuando la angustia y la angustia se apoderan de ti.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Entonces me llamarán, pero no responderé. Me buscarán con ahínco, pero no me encontrarán,
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 porque odiaban el conocimiento, y no eligió el temor a Yahvé.
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 No querían ningún consejo mío. Despreciaron toda mi reprimenda.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Por eso comerán del fruto de su propio camino, y se llenan de sus propios esquemas.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Porque la reincidencia de los simples los matará. La despreocupación de los tontos los destruirá.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Pero el que me escuche habitará con seguridad, y estarán tranquilos, sin temor a sufrir daños”.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”