< Números 31 >
1 Yahvé habló a Moisés, diciendo:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Véngate de los hijos de Israel contra los madianitas. Después te reunirás con tu pueblo”.
“Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
3 Moisés habló al pueblo diciendo: “Arma a los hombres de entre ustedes para la guerra, para que vayan contra Madián, para ejecutar la venganza de Yahvé contra Madián.
Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
4 Enviaréis mil de cada tribu, de todas las tribus de Israel, a la guerra.”
Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
5 Así que fueron entregados, de los miles de Israel, mil de cada tribu, doce mil armados para la guerra.
Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
6 Moisés los envió, mil de cada tribu, a la guerra con Finees, hijo del sacerdote Eleazar, a la guerra, con los utensilios santos del santuario y las trompetas de alarma en su mano.
Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
7 Lucharon contra Madián, como Yahvé le ordenó a Moisés. Mataron a todos los varones.
Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
8 Mataron a los reyes de Madián con el resto de sus muertos: Evi, Requem, Zur, Hur y Reba, los cinco reyes de Madián. También mataron a espada a Balaam, hijo de Beor.
Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
9 Los hijos de Israel tomaron cautivas a las mujeres de Madián con sus hijos, y tomaron como botín todo su ganado, todos sus rebaños y todos sus bienes.
Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
10 Quemaron todas sus ciudades en los lugares donde vivían y todos sus campamentos.
Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
11 Tomaron todos los cautivos y todo el botín, tanto de hombres como de animales.
Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
12 Llevaron a los cautivos, con la presa y el botín, a Moisés, al sacerdote Eleazar y a la congregación de los hijos de Israel, al campamento de los llanos de Moab, que están junto al Jordán, en Jericó.
Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
13 Moisés y el sacerdote Eleazar, con todos los jefes de la congregación, salieron a recibirlos fuera del campamento.
Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
14 Moisés se enojó con los oficiales del ejército, los capitanes de mil y los de cien, que venían del servicio de guerra.
Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
15 Moisés les dijo: “¿Habéis salvado a todas las mujeres con vida?
Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
16 He aquí que éstas hicieron que los hijos de Israel, por consejo de Balaam, cometieran transgresión contra Yahvé en el asunto de Peor, y así fue la plaga en la congregación de Yahvé.
Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
17 Maten, pues, a todo varón entre los pequeños, y maten a toda mujer que haya conocido al hombre acostándose con él.
Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
18 Pero todas las muchachas que no hayan conocido al hombre acostándose con él, manténganse vivas.
koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
19 “Acampad fuera del campamento durante siete días. El que haya matado a alguna persona, y el que haya tocado a algún muerto, purificaos al tercer día y al séptimo, vosotros y vuestros cautivos.
“Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
20 Purificaréis todos los vestidos, todo lo que sea de piel, todo lo que sea de pelo de cabra y todo lo que sea de madera.”
Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
21 El sacerdote Eleazar dijo a los hombres de guerra que iban a la batalla: “Este es el estatuto de la ley que Yahvé ha ordenado a Moisés.
Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
22 Sin embargo, el oro, la plata, el bronce, el hierro, el estaño y el plomo,
Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
23 todo lo que pueda resistir el fuego, lo haréis pasar por el fuego, y quedará limpio; no obstante, será purificado con el agua para la impureza. Todo lo que no resista el fuego lo harás pasar por el agua.
ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
24 El séptimo día lavarás tus ropas, y quedarás limpio. Después entrarás en el campamento”.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
25 Yahvé habló a Moisés, diciendo:
Yehova anawuza Mose kuti,
26 “Cuenta el botín que fue tomado, tanto de personas como de animales, tú, y el sacerdote Eleazar, y los jefes de familia de la congregación;
“Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
27 y divide el botín en dos partes: entre los hombres hábiles en la guerra, que salieron a la batalla, y toda la congregación.
Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
28 Levanten un tributo a Yahvé de los hombres de guerra que salieron a la batalla: un alma de cada quinientos; de las personas, del ganado, de los asnos y de los rebaños.
Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
29 Tómalo de la mitad de ellos y dáselo al sacerdote Eleazar, para la ofrenda mecida de Yahvé.
Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
30 De la mitad de los hijos de Israel, tomarás un alma de cada cincuenta, de las personas, del ganado, de los asnos y de los rebaños, de todo el ganado, y se los darás a los levitas, que cumplen con el deber del tabernáculo de Yahvé.”
Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
31 Moisés y el sacerdote Eleazar hicieron lo que Yahvé les ordenó.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
32 El botín, además del botín que tomaron los hombres de guerra, fue de seiscientas setenta y cinco mil ovejas,
Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
33 setenta y dos mil cabezas de ganado,
Ngʼombe 72,000,
34 sesenta y un mil asnos,
abulu 61,000,
35 y treinta y dos mil personas en total, de las mujeres que no habían conocido al hombre acostándose con él.
ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
36 La mitad, que era la porción de los que salían a la guerra, era en número de trescientas treinta y siete mil quinientas ovejas;
Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
37 y el tributo de las ovejas era de seiscientas setenta y cinco.
mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
38 El ganado vacuno era de treinta y seis mil, de los cuales el tributo de Yahvé era de setenta y dos.
ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
39 Los asnos eran treinta mil quinientos, de los cuales el tributo del Señor era sesenta y uno.
abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
40 Las personas eran dieciséis mil, de las cuales el tributo de Yahvé era de treinta y dos personas.
anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
41 Moisés entregó el tributo, que era la ofrenda mecida de Yahvé, al sacerdote Eleazar, como Yahvé se lo había ordenado a Moisés.
Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
42 De la mitad de los hijos de Israel, que Moisés repartió entre los hombres que combatieron
Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
43 (la mitad de la congregación era de trescientas treinta y siete mil quinientas ovejas,
Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
44 treinta y seis mil cabezas de ganado,
ngʼombe 36,000,
45 treinta mil quinientos asnos
abulu 30,500,
46 y dieciséis mil personas),
anthu 16,000.
47 de la mitad de los hijos de Israel, Moisés tomó un animal de cada cincuenta, tanto de hombres como de animales, y se los dio a los levitas, que cumplían con el deber del tabernáculo de Yahvé, como Yahvé le ordenó a Moisés.
Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
48 Se acercaron a Moisés los oficiales que estaban al frente de los miles del ejército, los capitanes de miles y los de cientos.
Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
49 Le dijeron a Moisés: “Tus siervos han tomado la suma de los hombres de guerra que están bajo nuestro mando, y no falta ni uno de nosotros.
iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
50 Hemos traído la ofrenda de Yahvé, lo que cada uno encontró: adornos de oro, brazaletes, pulseras, anillos de sello, pendientes y collares, para expiar nuestras almas ante Yahvé.”
Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
51 Moisés y el sacerdote Eleazar tomaron su oro, todas las joyas trabajadas.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
52 Todo el oro de la ofrenda de ola que ofrecieron a Yahvé, de los capitanes de millares y de los capitanes de centenas, fue de dieciséis mil setecientos cincuenta siclos.
Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
53 Los hombres de guerra habían tomado un botín, cada uno para sí mismo.
Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
54 Moisés y el sacerdote Eleazar tomaron el oro de los capitanes de millares y de centenas, y lo llevaron a la Tienda del Encuentro como memorial para los hijos de Israel ante Yahvé.
Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.