< Números 26 >
1 Después de la plaga, Yahvé habló a Moisés y al sacerdote Eleazar hijo de Aarón, diciendo:
Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
2 “Hagan un censo de toda la congregación de los hijos de Israel, de veinte años en adelante, por las casas de sus padres, todos los que puedan salir a la guerra en Israel.”
“Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
3 Moisés y el sacerdote Eleazar hablaron con ellos en las llanuras de Moab, junto al Jordán, en Jericó, diciendo:
Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
4 “Hagan un censo, de veinte años en adelante, como Yahvé les ordenó a Moisés y a los hijos de Israel.” Estos son los que salieron de la tierra de Egipto.
“Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
5 Rubén, el primogénito de Israel; los hijos de Rubén: de Hanoc, la familia de los Hanocitas; de Falú, la familia de los Falúitas;
Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
6 de Esrom, la familia de los Esromitas; de Carmi, la familia de los Carmitas.
kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
7 Estas son las familias de los rubenitas; y los contados de ellas fueron cuarenta y tres mil setecientos treinta.
Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
8 El hijo de Pallu: Eliab.
Mwana wa Palu anali Eliabu,
9 Los hijos de Eliab: Nemuel, Datán y Abiram. Estos son aquellos Datán y Abiram que fueron llamados por la congregación, que se rebelaron contra Moisés y contra Aarón en la compañía de Coré cuando se rebelaron contra Yahvé;
ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
10 y la tierra abrió su boca y los tragó junto con Coré cuando esa compañía murió; en ese momento el fuego devoró a doscientos cincuenta hombres, y se convirtieron en una señal.
Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
11 Sin embargo, los hijos de Coré no murieron.
Koma ana a Kora sanafe nawo.
12 Los hijos de Simeón por sus familias: de Nemuel, la familia de los nemuelitas; de Jamín, la familia de los jaminitas; de Jaquín, la familia de los jaquinitas;
Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
13 de Zera, la familia de los zeraítas; de Saúl, la familia de los shaúlitas.
kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
14 Estas son las familias de los simeonitas, veintidós mil doscientos.
Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
15 Los hijos de Gad por sus familias: de Zefón, la familia de los zefonitas; de Haggi, la familia de los haggitas; de Suni, la familia de los sunitas;
Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
16 de Ozni, la familia de los oznitas; de Eri, la familia de los eritas;
kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
17 de Arod, la familia de los aroditas; de Areli, la familia de los arelitas.
kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
18 Estas son las familias de los hijos de Gad según los contados de ellos, cuarenta mil quinientos.
Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
19 Los hijos de Judá: Er y Onán. Er y Onán murieron en la tierra de Canaán.
Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
20 Los hijos de Judá por sus familias fueron: de Selá, la familia de los selanitas; de Fares, la familia de los pérezicos; de Zera, la familia de los zeraitas.
Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
21 Los hijos de Fares fueron: de Esrom, la familia de los Esromitas; de Hamul, la familia de los hamulitas.
Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
22 Estas son las familias de Judá según los contados de ellas, setenta y seis mil quinientos.
Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
23 Los hijos de Isacar por sus familias: de Tola, la familia de los tolaítas; de Puva, la familia de los punítas;
Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
24 de Jasub, la familia de los jasubitas; de Simrón, la familia de los simronitas.
kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
25 Estas son las familias de Isacar según los contados de ellas, sesenta y cuatro mil trescientos.
Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
26 Los hijos de Zabulón por sus familias: de Sered, la familia de los sereditas; de Elón, la familia de los elonitas; de Jahleel, la familia de los jahleelitas.
Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
27 Estas son las familias de los zabulonitas según los contados de ellos, sesenta mil quinientos.
Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
28 Los hijos de José según sus familias: Manasés y Efraín.
Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
29 Los hijos de Manasés: de Maquir, la familia de los maquiritas; y Maquir fue el padre de Galaad; de Galaad, la familia de los galaaditas.
Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
30 Estos son los hijos de Galaad: de Jezer, la familia de los Jezeritas; de Helec, la familia de los Helequitas;
Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
31 y de Asriel, la familia de los Asrielitas; y de Siquem, la familia de los Siquemitas;
kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
32 y de Semida, la familia de los Semidaitas; y de Hefer, la familia de los Heferitas.
kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
33 Zelofehad, hijo de Hefer, no tuvo hijos, sino hijas; y los nombres de las hijas de Zelofehad fueron Maalá, Noa, Hogiá, Milca y Tirsa.
(Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
34 Estas son las familias de Manasés. Los contados de ellos fueron cincuenta y dos mil setecientos.
Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
35 Estos son los hijos de Efraín por sus familias: de Sutela, la familia de los Sutelitas; de Bequer, la familia de los Bequeritas; de Tahan, la familia de los Tahanitas.
Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
36 Estos son los hijos de Sutela: de Erán, la familia de los eranitas.
Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
37 Estas son las familias de los hijos de Efraín, según los contados de ellos, treinta y dos mil quinientos. Estos son los hijos de José por sus familias.
Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
38 Los hijos de Benjamín por sus familias: de Bela, la familia de los belaítas; de Asbel, la familia de los asbelitas; de Ahiram, la familia de los ahiramitas;
Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
39 de Sefufam, la familia de los sefufamitas; de Hufam, la familia de los hufamitas.
kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
40 Los hijos de Bela fueron Ard y Naamán: la familia de los arditas; y de Naamán, la familia de los naamitas.
Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
41 Estos son los hijos de Benjamín por sus familias; y los contados de ellos fueron cuarenta y cinco mil seiscientos.
Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
42 Estos son los hijos de Dan por sus familias: de Suham, la familia de los suhamitas. Estas son las familias de Dan por sus familias.
Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
43 Todas las familias de los suhamitas, según los contados de ellos, fueron sesenta y cuatro mil cuatrocientos.
Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
44 Los hijos de Aser por sus familias: de Imna, la familia de los imnitas; de Imna, la familia de los imnitas; de Beriá, la familia de los beritas.
Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
45 De los hijos de Beriá: de Heber, la familia de los heberitas; de Malquiel, la familia de los malquielitas.
ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
46 El nombre de la hija de Aser fue Sera.
(Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
47 Estas son las familias de los hijos de Aser según los contados de ellos, cincuenta y tres mil cuatrocientos.
Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
48 Los hijos de Neftalí por sus familias: de Jahzeel, la familia de los jahzeelitas; de Guni, la familia de los gunitas;
Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
49 de Jezer, la familia de los jezeritas; de Silem, la familia de los silemitas.
kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
50 Estas son las familias de Neftalí según sus familias; y los contados de ellas fueron cuarenta y cinco mil cuatrocientos.
Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
51 Estos son los contados de los hijos de Israel, seiscientos un mil setecientos treinta.
Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
52 Yahvé habló a Moisés diciendo:
Yehova anawuza Mose kuti,
53 “A éstos se les repartirá la tierra en herencia según el número de nombres.
“Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
54 A los más les darás más herencia, y a los menos les darás menos herencia. A cada uno se le dará su herencia según los contados de él.
Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
55 Sin embargo, la tierra se dividirá por sorteo. Según los nombres de las tribus de sus padres heredarán.
Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
56 Según la suerte se repartirá su herencia entre los más y los menos”.
Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
57 Estos son los contados de los levitas según sus familias: de Gersón, la familia de los gersonitas; de Coat, la familia de los coatitas; de Merari, la familia de los meraritas.
Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
58 Estas son las familias de Leví: la familia de los libnitas, la familia de los hebronitas, la familia de los mahlitas, la familia de los musitas y la familia de los coreitas. Coat fue el padre de Amram.
Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
59 El nombre de la esposa de Amram era Jocabed, hija de Leví, que había nacido de Leví en Egipto. Ella dio a luz a Amram, a Aarón y a Moisés, y a su hermana Miriam.
Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
60 De Aarón nacieron Nadab y Abiú, Eleazar e Itamar.
Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
61 Nadab y Abiú murieron cuando ofrecieron fuego extraño ante Yahvé.
Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
62 Los que fueron contados de ellos fueron veintitrés mil, todos los varones de un mes para arriba; pues no fueron contados entre los hijos de Israel, porque no se les dio herencia entre los hijos de Israel.
Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
63 Estos son los que fueron contados por Moisés y el sacerdote Eleazar, quienes contaron a los hijos de Israel en los llanos de Moab, junto al Jordán de Jericó.
Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
64 Pero entre éstos no hubo ninguno de los que fueron contados por Moisés y el sacerdote Aarón, que contaron a los hijos de Israel en el desierto de Sinaí.
Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
65 Porque Yahvé había dicho de ellos: “Ciertamente morirán en el desierto”. No quedó ningún hombre de ellos, excepto Caleb, hijo de Jefone, y Josué, hijo de Nun.
Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.