< Jueces 10 >
1 Después de Abimelec, Tola, hijo de Puah, hijo de Dodo, un hombre de Isacar, se levantó para salvar a Israel. Vivió en Shamir, en la región montañosa de Efraín.
Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
2 Juzgó a Israel durante veintitrés años, murió y fue enterrado en Samir.
Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
3 Después de él se levantó Jair, el Galaadita. Juzgó a Israel durante veintidós años.
Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
4 Tenía treinta hijos que montaban en treinta asnos. Tenían treinta ciudades, que hasta hoy se llaman Havvoth Jair, que están en el país de Galaad.
Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
5 Jair murió y fue enterrado en Kamon.
Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
6 Los hijos de Israel volvieron a hacer lo que era malo a los ojos de Yahvé, y sirvieron a los baales, a Astarot, a los dioses de Siria, a los dioses de Sidón, a los dioses de Moab, a los dioses de los hijos de Amón y a los dioses de los filisteos. Abandonaron a Yahvé y no le sirvieron.
Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
7 La ira de Yahvé ardió contra Israel, y lo vendió en manos de los filisteos y de los hijos de Amón.
Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
8 Aquel año molestaron y oprimieron a los hijos de Israel. Durante dieciocho años oprimieron a todos los hijos de Israel que estaban al otro lado del Jordán, en la tierra de los amorreos, que está en Galaad.
Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
9 Los hijos de Amón pasaron el Jordán para luchar también contra Judá, contra Benjamín y contra la casa de Efraín, de modo que Israel estaba muy afligido.
Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
10 Los hijos de Israel clamaron a Yahvé diciendo: “Hemos pecado contra ti, porque hemos abandonado a nuestro Dios y hemos servido a los baales.”
Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
11 El Señor dijo a los hijos de Israel: “¿No os salvé de los egipcios, de los amorreos, de los hijos de Amón y de los filisteos?
Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
12 También os oprimieron los sidonios, los amalecitas y los maonitas; y vosotros clamasteis a mí, y yo os salvé de su mano.
Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
13 Pero me habéis abandonado y habéis servido a otros dioses. Por eso no os salvaré más.
Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
14 Ve y clama a los dioses que has elegido. Que te salven en el momento de tu angustia”.
Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
15 Los hijos de Israel dijeron a Yahvé: “¡Hemos pecado! Haz con nosotros lo que te parezca bien; sólo líbranos, por favor, hoy”.
Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
16 Abandonaron los dioses extranjeros de entre ellos y sirvieron a Yahvé; y su alma se entristeció por la miseria de Israel.
Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
17 Entonces los hijos de Amón se reunieron y acamparon en Galaad. Los hijos de Israel se reunieron y acamparon en Mizpa.
Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
18 El pueblo, los príncipes de Galaad, se dijeron unos a otros: “¿Quién es el hombre que comenzará a luchar contra los hijos de Amón? Él será el jefe de todos los habitantes de Galaad”.
Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”