< Josué 21 >
1 Los jefes de familia de los levitas se acercaron al sacerdote Eleazar, a Josué hijo de Nun y a los jefes de familia de las tribus de los hijos de Israel.
Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
2 Les hablaron en Silo, en la tierra de Canaán, diciendo: “Yahvé ordenó por medio de Moisés que nos dieran ciudades para habitar, con sus tierras de pastoreo para nuestro ganado.”
ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
3 Los hijos de Israel dieron a los levitas, de su herencia, según el mandato de Yahvé, estas ciudades con sus tierras de pastoreo.
Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
4 La suerte salió para las familias de los coatitas. Los hijos del sacerdote Aarón, que eran de los levitas, tuvieron trece ciudades por sorteo de la tribu de Judá, de la tribu de los simeonitas y de la tribu de Benjamín.
Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
5 Los demás hijos de Coat tenían diez ciudades por sorteo de las familias de la tribu de Efraín, de la tribu de Dan y de la media tribu de Manasés.
Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
6 Los hijos de Gersón tuvieron trece ciudades por sorteo de las familias de la tribu de Isacar, de la tribu de Aser, de la tribu de Neftalí y de la media tribu de Manasés en Basán.
Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
7 Los hijos de Merari, según sus familias, tenían doce ciudades de la tribu de Rubén, de la tribu de Gad y de la tribu de Zabulón.
Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
8 Los hijos de Israel dieron estas ciudades con sus tierras de pastoreo por sorteo a los levitas, como lo ordenó el Señor por medio de Moisés.
Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
9 Dieron de la tribu de los hijos de Judá, y de la tribu de los hijos de Simeón, estas ciudades que se mencionan por su nombre:
Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
10 y fueron para los hijos de Aarón, de las familias de los coatitas, que eran de los hijos de Leví; porque de ellos fue la primera suerte.
ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
11 Les dieron Quiriat Arba, llamada así por el padre de Anac (también llamada Hebrón), en la región montañosa de Judá, con sus tierras de pastoreo alrededor.
Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
12 Pero dieron los campos de la ciudad y sus aldeas a Caleb, hijo de Jefone, para su posesión.
Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
13 A los hijos del sacerdote Aarón les dieron Hebrón con sus tierras de pastoreo, la ciudad de refugio para el matador de hombres, Libna con sus tierras de pastoreo,
Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
14 Jattir con sus tierras de pastoreo, Estemoa con sus tierras de pastoreo,
Yatiri, Esitemowa,
15 Holón con sus tierras de pastoreo, Debir con sus tierras de pastoreo,
Holoni, Debri,
16 Ain con sus tierras de pastoreo, Jutá con sus tierras de pastoreo y Bet Semes con sus tierras de pastoreo: nueve ciudades de esas dos tribus.
Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
17 De la tribu de Benjamín, Gabaón con sus tierras de pastoreo, Geba con sus tierras de pastoreo,
Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
18 Anatot con sus tierras de pastoreo y Almón con sus tierras de pastoreo: cuatro ciudades.
Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
19 Todas las ciudades de los hijos de Aarón, los sacerdotes, eran trece ciudades con sus tierras de pastoreo.
Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
20 Las familias de los hijos de Coat, los levitas, el resto de los hijos de Coat, tuvieron las ciudades de su lote de la tribu de Efraín.
Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
21 Les dieron Siquem con sus tierras de pastoreo en la región montañosa de Efraín, la ciudad de refugio para el matador de hombres, y Gezer con sus tierras de pastoreo,
Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
22 Kibzaim con sus tierras de pastoreo, y Bet Horón con sus tierras de pastoreo: cuatro ciudades.
Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
23 De la tribu de Dan, Elteke con sus tierras de pastoreo, Gibetón con sus tierras de pastoreo,
Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
24 Ajalón con sus tierras de pastoreo, Gat Rimón con sus tierras de pastoreo: cuatro ciudades.
Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
25 De la media tribu de Manasés, Taanac con sus tierras de pastoreo y Gat Rimón con sus tierras de pastoreo: dos ciudades.
Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
26 Todas las ciudades de las familias del resto de los hijos de Coat fueron diez con sus tierras de pastoreo.
Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
27 Dieron a los hijos de Gersón, de las familias de los levitas, de la media tribu de Manasés, Golán en Basán con sus tierras de pastoreo, la ciudad de refugio para el matador de hombres, y Be Esterá con sus tierras de pastoreo: dos ciudades.
Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
28 De la tribu de Isacar, Kishion con sus tierras de pastoreo, Daberat con sus tierras de pastoreo,
Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
29 Jarmut con sus tierras de pastoreo, En Gannim con sus tierras de pastoreo: cuatro ciudades.
Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
30 De la tribu de Aser, Mishal con sus tierras de pastoreo, Abdón con sus tierras de pastoreo,
Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
31 Helkat con sus tierras de pastoreo, y Rehob con sus tierras de pastoreo: cuatro ciudades.
Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
32 De la tribu de Neftalí, Cedes en Galilea con sus tierras de pastoreo, la ciudad de refugio para el matador de hombres, Hamotdor con sus tierras de pastoreo y Kartán con sus tierras de pastoreo: tres ciudades.
Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
33 Todas las ciudades de los gersonitas, según sus familias, eran trece ciudades con sus tierras de pastoreo.
Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
34 A las familias de los hijos de Merari, el resto de los levitas, de la tribu de Zabulón, Jocneam con sus tierras de pastoreo, Kartah con sus tierras de pastoreo,
Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
35 Dimna con sus tierras de pastoreo y Nahalal con sus tierras de pastoreo: cuatro ciudades.
Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
36 De la tribu de Rubén, Beser con sus tierras de pastoreo, Jahaz con sus tierras de pastoreo,
Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
37 Cedemot con sus tierras de pastoreo, y Mefat con sus tierras de pastoreo: cuatro ciudades.
Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
38 De la tribu de Gad, Ramot en Galaad con sus tierras de pastoreo, la ciudad de refugio para el matador de hombres, y Mahanaim con sus tierras de pastoreo,
Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
39 Hesbón con sus tierras de pastoreo, Jazer con sus tierras de pastoreo: cuatro ciudades en total.
Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
40 Todas estas fueron las ciudades de los hijos de Merari según sus familias, el resto de las familias de los levitas. Su suerte fue de doce ciudades.
Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
41 Todas las ciudades de los levitas entre las posesiones de los hijos de Israel eran cuarenta y ocho ciudades con sus tierras de pastoreo.
Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
42 Cada una de estas ciudades incluía sus tierras de pastoreo alrededor de ellas. Así fue con todas estas ciudades.
Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
43 El Señor dio a Israel toda la tierra que había jurado dar a sus padres. La poseyeron y vivieron en ella.
Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
44 El Señor les dio descanso en todo el territorio, según lo que había jurado a sus padres. Ni un solo hombre de todos sus enemigos se presentó ante ellos. El Señor entregó a todos sus enemigos en sus manos.
Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
45 No faltó nada de lo bueno que el Señor había dicho a la casa de Israel. Todo se cumplió.
Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.