< Joel 2 >

1 Toca la trompeta en Sión, ¡y hacer sonar una alarma en mi montaña sagrada! Que tiemblen todos los habitantes de la tierra, porque llega el día de Yahvé, porque está muy cerca:
Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
2 Un día de oscuridad y penumbra, un día de nubes y espesa oscuridad. Como el amanecer que se extiende sobre las montañas, un pueblo grande y fuerte; nunca ha habido algo parecido, ni habrá más después de ellos, incluso a los años de muchas generaciones.
tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
3 Un fuego devora ante ellos, y detrás de ellos, arde una llama. La tierra es como el jardín del Edén ante ellos, y detrás de ellos, un desierto desolado. Sí, y nadie ha escapado de ellos.
Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
4 Su aspecto es como el de los caballos, y corren como jinetes.
Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
5 Como el ruido de los carros en las cimas de los montes, saltan, como el ruido de una llama de fuego que devora el rastrojo, como un pueblo fuerte puesto en orden de batalla.
Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
6 Ante su presencia los pueblos se angustian. Todos los rostros se han vuelto pálidos.
Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
7 Corren como hombres poderosos. Escalan el muro como guerreros. Cada uno de ellos marcha en su línea, y no se desvían del camino.
Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
8 Uno no empuja a otro. Cada uno marcha por su propio camino. Rompieron las defensas y no rompan filas.
Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
9 Se precipitan sobre la ciudad. Corren en la pared. Suben a las casas. Entran por las ventanas como ladrones.
Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
10 La tierra tiembla ante ellos. Los cielos tiemblan. El sol y la luna se oscurecen, y las estrellas retiran su brillo.
Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
11 Yahvé hace tronar su voz ante su ejército, porque sus fuerzas son muy grandes; porque es fuerte quien obedece su mandato; porque el día de Yahvé es grande y muy imponente, ¿y quién puede soportarlo?
Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
12 “Sin embargo, ahora mismo — dice Yahvé — vuélvete a mí con todo tu corazón, y con ayuno, llanto y luto”.
“Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
13 Rasga tu corazón y no tus vestiduras, y vuélvete a Yahvé, tu Dios; porque es clemente y misericordioso, lento para la ira, y abundante en bondad amorosa, y se abstiene de enviar la calamidad.
Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
14 ¿Quién sabe? Puede que se vuelva y ceda, y dejar una bendición detrás de él, una ofrenda de comida y una ofrenda de bebida a Yahvé, tu Dios.
Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
15 ¡Toca la trompeta en Sión! Santificar un ayuno. Convocar una asamblea solemne.
Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
16 Reúne al pueblo. Santificar la asamblea. Reúne a los ancianos. Reúne a los niños, y a los que amamantan de pecho. Que el novio salga de su habitación, y la novia fuera de su cámara.
Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
17 Que los sacerdotes, los ministros de Yahvé, lloren entre el pórtico y el altar, y que digan: “Perdona a tu pueblo, Yahvé, y no des tu herencia a los reproches, que las naciones se enseñoreen de ellos. ¿Por qué han de decir entre los pueblos, ¿Dónde está su Dios?”
Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
18 Entonces Yahvé se puso celoso por su tierra, y se apiadó de su pueblo.
Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
19 Yahvé respondió a su pueblo, “Mira, te enviaré grano, vino nuevo y aceite, y estarás satisfecho con ellos; y no volveré a hacer de ti un oprobio entre las naciones.
Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
20 Pero yo alejaré de ti al ejército del norte, y lo conducirá a una tierra estéril y desolada, su frente en el mar del este, y su espalda en el mar occidental; y su hedor surgirá, y su mal olor se elevará”. Seguro que ha hecho grandes cosas.
“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
21 Tierra, no tengas miedo. Alegraos y regocijaos, porque Yahvé ha hecho grandes cosas.
Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
22 No tengáis miedo, animales del campo; porque los pastos del desierto brotan, porque el árbol da sus frutos. La higuera y la vid dan su fuerza.
Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
23 “Alegraos, pues, hijos de Sión, y alégrate en Yahvé, tu Dios; pues te da la lluvia temprana en justa medida, y hace que la lluvia caiga para ti, la lluvia temprana y la lluvia tardía, como antes.
Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 Las eras estarán llenas de trigo, y las cubas rebosarán de vino nuevo y aceite.
Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
25 Te devolveré los años que se ha comido la langosta, la gran langosta, el saltamontes y la oruga, mi gran ejército, que envié entre vosotros.
“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 Tendrás mucho que comer y estarás satisfecho, y alabarán el nombre de Yahvé, su Dios, que ha tratado maravillosamente contigo; y mi pueblo nunca más será decepcionado.
Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 Sabrás que estoy en medio de Israel, y que yo soy Yahvé, tu Dios, y no hay otro; y mi pueblo nunca más será decepcionado.
Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
28 “Después sucederá que derramaré mi Espíritu sobre toda la carne; y tus hijos y tus hijas profetizarán. Tus viejos soñarán sueños. Sus jóvenes verán visiones.
“Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
29 Y también sobre los siervos y las siervas en aquellos días, Derramaré mi Espíritu.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 Mostraré maravillas en los cielos y en la tierra: sangre, fuego y columnas de humo.
Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 El sol se convertirá en oscuridad, y la luna en sangre, antes de que llegue el gran y terrible día de Yahvé.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 Sucederá que quien invoque el nombre de Yahvé se salvará; porque en el monte Sión y en Jerusalén habrá quienes escapen, como ha dicho Yahvé, y entre el remanente, los que Yahvé llama.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.

< Joel 2 >