< Job 5 >
1 “Llama ahora; ¿hay alguien que te responda? ¿A cuál de los santos te dirigirás?
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Porque el resentimiento mata al necio, y los celos matan a los simples.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 He visto a los insensatos echar raíces, pero de repente maldije su morada.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 Sus hijos están lejos de la seguridad. Son aplastados en la puerta. Tampoco hay ninguno que los entregue,
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 cuya cosecha devoran los hambrientos, y sacarlo incluso de las espinas. La trampa se abre para su sustancia.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Porque la aflicción no sale del polvo, tampoco los problemas surgen de la tierra;
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 pero el hombre ha nacido para el problema, mientras las chispas vuelan hacia arriba.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 “Pero en cuanto a mí, buscaría a Dios. Yo encomendaría mi causa a Dios,
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 que hace grandes cosas que no se pueden comprender, cosas maravillosas sin número;
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 que hace llover sobre la tierra, y envía aguas sobre los campos;
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 para que ponga en alto a los de abajo, los que lloran son exaltados a la seguridad.
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Él frustra los planes de los astutos, para que sus manos no puedan realizar su empresa.
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 El toma a los sabios en su propia astucia; el consejo de los astutos se lleva de cabeza.
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 Se encuentran con la oscuridad durante el día, y tantear al mediodía como en la noche.
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Pero él salva de la espada de su boca, incluso a los necesitados de la mano de los poderosos.
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Así que el pobre tiene esperanza, y la injusticia le cierra la boca.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 “He aquí que es feliz el hombre a quien Dios corrige. Por lo tanto, no desprecies el castigo del Todopoderoso.
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Porque él hiere y venda. Se hiere y sus manos se recomponen.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Él te librará en seis problemas; sí, en siete ningún mal te tocará.
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 En el hambre te reducirá de la muerte; en la guerra, del poder de la espada.
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Estarás oculto del azote de la lengua, ni tendrás miedo de la destrucción cuando llegue.
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Te reirás de la destrucción y del hambre, ni tendrás miedo de los animales de la tierra.
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 Porque serás aliado de las piedras del campo. Los animales del campo estarán en paz contigo.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Sabrás que tu tienda está en paz. Visitarás tu redil y no echarás nada en falta.
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 También sabrás que tu descendencia será grande, tu descendencia como la hierba de la tierra.
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Llegarás a la tumba en plena edad, como una descarga de grano viene en su temporada.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 He aquí que lo hemos investigado. Así es. Escúchalo y conócelo para tu bien”.
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”