< Job 38 >
1 Entonces Yahvé respondió a Job desde el torbellino,
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 “¿Quién es el que oscurece el consejo por palabras sin conocimiento?
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Prepárate como un hombre, porque yo te interrogaré y tú me responderás.
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 “¿Dónde estabas cuando puse los cimientos de la tierra? Declara, si tienes entendimiento.
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 ¿Quién determinó sus medidas, si lo sabe? ¿O quién estiró la línea en él?
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 ¿Sobre qué estaban fijados sus cimientos? O quién puso su piedra angular,
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 cuando las estrellas de la mañana cantaban juntas, y todos los hijos de Dios gritaron de alegría?
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 “O que cierra el mar con puertas, cuando salió del vientre materno,
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 cuando hice de las nubes su vestimenta, y lo envolvió en una espesa oscuridad,
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 marcadas para ello mi límite, poner barras y puertas,
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 y dijo: “Puedes venir aquí, pero no más allá. ¿Tus orgullosas olas serán detenidas aquí?
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 “¿Has ordenado la mañana en tus días, y ha hecho que el amanecer conozca su lugar,
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 para que se apodere de los confines de la tierra, y sacudir a los malvados fuera de ella?
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 Se cambia como la arcilla bajo el sello, y presentado como una prenda de vestir.
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 A los malvados se les oculta la luz. El brazo alto está roto.
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 “¿Has entrado en los manantiales del mar? ¿O has caminado por los recovecos de las profundidades?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 ¿Se te han revelado las puertas de la muerte? ¿O has visto las puertas de la sombra de la muerte?
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 ¿Has comprendido la tierra en su anchura? Declara, si lo sabes todo.
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 “¿Cuál es el camino hacia la morada de la luz? En cuanto a la oscuridad, cuál es su lugar,
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 que lo lleves a su límite, para que discierna los caminos de su casa?
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 Seguramente lo sabes, pues naciste entonces, ¡y el número de sus días es genial!
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 ¿Has entrado en los almacenes de la nieve, o has visto los almacenes del granizo,
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 que he reservado para el tiempo de la angustia, contra el día de la batalla y la guerra?
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 De qué manera se distribuye el rayo, o el viento del este disperso en la tierra?
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Que ha cortado un canal para el agua de la inundación, o la trayectoria de la tormenta,
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 para hacer llover en una tierra donde no hay hombre, en el desierto, en el que no hay hombre,
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 para saciar el terreno baldío y desolado, para hacer crecer la hierba tierna?
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 ¿La lluvia tiene padre? ¿O quién recoge las gotas de rocío?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 ¿De qué vientre salió el hielo? ¿Quién ha dado a luz a la escarcha gris del cielo?
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 Las aguas se vuelven duras como la piedra, cuando la superficie de las profundidades está congelada.
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 “¿Puedes atar el cúmulo de las Pléyades, o aflojar las cuerdas de Orión?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 ¿Puedes guiar a las constelaciones en su estación? ¿O puedes guiar a la Osa con sus cachorros?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 ¿Conoces las leyes de los cielos? ¿Puede establecer su dominio sobre la tierra?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 “¿Puedes elevar tu voz a las nubes, para que la abundancia de aguas te cubra?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 ¿Puedes enviar relámpagos para que se vayan? ¿Te informan de que “aquí estamos”?
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 ¿Quién ha puesto la sabiduría en las partes interiores? ¿O quién ha dado entendimiento a la mente?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 ¿Quién puede contar las nubes con sabiduría? O que puede verter los contenedores del cielo,
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 cuando el polvo se convierte en una masa, y los terrones se pegan?
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 “¿Puedes cazar la presa para la leona, o satisfacer el apetito de los jóvenes leones,
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 cuando se agazapan en sus guaridas, y acechar en la espesura?
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Que proporciona al cuervo su presa, cuando sus jóvenes claman a Dios, y vagan por falta de comida?
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?