< Job 31 >
1 “Hice un pacto con mis ojos; ¿cómo debería entonces mirar con lujuria a una mujer joven?
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 Porque lo que es la porción de Dios en lo alto, y la herencia del Todopoderoso en las alturas?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 ¿No es una calamidad para los injustos, y el desastre a los obreros de la iniquidad?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 No ve mis caminos, y contar todos mis pasos?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 “Si he andado con falsedad, y mi pie se ha apresurado a engañar
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 (que me pesen en una balanza uniforme, para que Dios conozca mi integridad);
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 si mi paso se ha desviado del camino, si mi corazón caminara tras mis ojos, si alguna mancha se ha pegado a mis manos,
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 entonces déjame sembrar, y que otro coma. Sí, que el producto de mi campo sea desarraigado.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 “Si mi corazón ha sido seducido por una mujer, y he esperado en la puerta de mi vecino,
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 que muela para otro mi mujer, y otros se encorven sobre ella.
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 Porque eso sería un crimen atroz. Sí, sería una iniquidad ser castigado por los jueces,
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 porque es un fuego que consume hasta la destrucción, y que me arrancaría de raíz todo mi aumento.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 “Si he despreciado la causa de mi siervo o de mi sirvienta, cuando contendían conmigo,
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 ¿Qué haré entonces cuando Dios se levante? Cuando me visite, ¿qué le responderé?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 ¿Acaso no lo hizo el que me hizo en el vientre? ¿No se nos formó en el vientre materno?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 “Si he retenido a los pobres de su deseo, o han hecho fallar los ojos de la viuda,
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 o haber comido mi bocado solo, y el huérfano no ha comido de ella
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 (no, desde mi juventud creció conmigo como con un padre, La he guiado desde el vientre de mi madre);
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 si he visto a alguno perecer por falta de ropa, o que los necesitados no tenían cobertura;
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 si su corazón no me ha bendecido, si no se ha calentado con el vellón de mi oveja;
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 si he levantado mi mano contra los huérfanos, porque vi mi ayuda en la puerta;
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 entonces dejé caer mi hombro desde el omóplato, y que mi brazo se rompa desde el hueso.
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 Porque la calamidad de Dios es un terror para mí. Por su majestad, no puedo hacer nada.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 “Si he hecho del oro mi esperanza, y han dicho al oro fino: “Tú eres mi confianza”.
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 Si me he alegrado porque mi riqueza era grande, y porque mi mano se había vuelto mucho;
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 si he visto el sol cuando brillaba, o la luna moviéndose con esplendor,
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 y mi corazón ha sido seducido en secreto, y mi mano lanzó un beso de mi boca;
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 esto también sería una iniquidad que sería castigada por los jueces, porque habría negado al Dios que está arriba.
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 “Si me he alegrado de la destrucción del que me odiaba, o me levanté cuando el mal lo encontró
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 (Ciertamente no he permitido que mi boca peque pidiendo su vida con una maldición);
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 si los hombres de mi tienda no han dicho, ¿Quién puede encontrar a alguien que no se haya saciado con su carne?
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 (el extranjero no ha acampado en la calle, pero he abierto mis puertas al viajero);
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 si como Adán he cubierto mis transgresiones, ocultando mi iniquidad en mi corazón,
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 porque temía a la gran multitud, y el desprecio de las familias me aterrorizó, así que guardé silencio, y no salí de la puerta...
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 ¡ojalá tuviera uno que me escuchara! ¡He aquí mi firma! ¡Que el Todopoderoso me responda! ¡Que el acusador escriba mi acusación!
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Seguramente lo llevaría al hombro, y lo ataría a mí como una corona.
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 Yo le declararía el número de mis pasos. Me acercaría a él como un príncipe.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 Si mi tierra grita contra mí, y sus surcos lloran juntos;
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 si he comido sus frutos sin dinero, o han hecho que sus propietarios pierdan la vida,
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 deja que los cardoscrezcan en lugar del trigo, y stinkweed en lugar de cebada”. Las palabras de Job han terminado.
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.