< Job 29 >
1 Job retomó su parábola y dijo
Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 “Oh, si yo fuera como en los meses de antaño, como en los días en que Dios velaba por mí;
“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
3 cuando su lámpara brilló sobre mi cabeza, y con su luz atravesé las tinieblas,
pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
4 como estaba en mi mejor momento, cuando la amistad de Dios estaba en mi tienda,
Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
5 cuando el Todopoderoso aún estaba conmigo, y mis hijos estaban a mi alrededor,
nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
6 cuando mis pasos fueron lavados con mantequilla, y la roca derramó chorros de aceite para mí,
pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
7 cuando salí a la puerta de la ciudad, cuando preparé mi asiento en la calle.
“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
8 Los jóvenes me vieron y se escondieron. Los ancianos se levantaron y se pusieron de pie.
anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
9 Los príncipes se abstuvieron de hablar, y se puso la mano en la boca.
atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
10 La voz de los nobles se acalló, y su lengua se pegó al paladar.
anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
11 Porque cuando el oído me escuchó, entonces me bendijo, y cuando el ojo me vio, me elogió,
Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
12 porque liberé a los pobres que lloraban, y también al huérfano, que no tenía quien le ayudara,
chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
13 la bendición del que estaba dispuesto a perecer vino sobre mí, y he hecho que el corazón de la viuda cante de alegría.
Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
14 Me vestí de justicia, y me vistió. Mi justicia era como un manto y una diadema.
Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
15 Yo era los ojos de los ciegos, y los pies a los cojos.
Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
16 Fui padre de los necesitados. Investigué la causa de él que no conocía.
Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
17 Rompí las mandíbulas de los injustos y arrancó la presa de sus dientes.
Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
18 Entonces dije: “Moriré en mi propia casa, Contaré mis días como la arena.
“Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
19 Mi raíz se extiende hasta las aguas. El rocío reposa toda la noche en mi rama.
Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
20 Mi gloria está fresca en mí. Mi arco se renueva en mi mano’.
Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
21 “Los hombres me escucharon, esperaron, y guardé silencio por mi consejo.
“Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
22 Después de mis palabras no volvieron a hablar. Mi discurso cayó sobre ellos.
Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
23 Me esperaron como a la lluvia. Sus bocas bebieron como con la lluvia de primavera.
Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
24 Les sonreí cuando no tenían confianza. No rechazaron la luz de mi rostro.
Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
25 elegí fuera de su camino, y me senté como jefe. Viví como un rey en el ejército, como quien consuela a los dolientes.
Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”