< Job 17 >
1 “Mi espíritu se consume. Mis días se extinguen y la tumba está lista para mí.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 Seguramente hay burlones conmigo. Mi ojo se detiene en su provocación.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 “Ahora da una prenda. Sé un aval para mí con tu persona. ¿Quién es el que se da la mano conmigo?
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 Porque has ocultado su corazón al entendimiento, por lo que no los exaltarás.
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 El que denuncia a sus amigos por el despojo, hasta los ojos de sus hijos fallarán.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 “Pero él me ha convertido en un sinónimo del pueblo. Me escupen en la cara.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 También mi ojo se oscurece a causa del dolor. Todos mis miembros son como una sombra.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 Los hombres rectos se asombrarán de esto. El inocente se revolverá contra el impío.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 Pero el justo se mantendrá en su camino. El que tiene las manos limpias se hará cada vez más fuerte.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 Pero en cuanto a ustedes, vuelvan. No encontraré un hombre sabio entre vosotros.
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 Mis días han pasado. Mis planes se han roto, como los pensamientos de mi corazón.
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 Algunos convierten la noche en día, diciendo: “La luz está cerca”, en presencia de las tinieblas.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 Si busco el Seol como mi casa, si he extendido mi sofá en las tinieblas, (Sheol )
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol )
14 si he dicho a la corrupción: “Tú eres mi padre y al gusano: “Mi madre” y “Mi hermana”.
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 ¿dónde está entonces mi esperanza? En cuanto a mi esperanza, ¿quién la verá?
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 ¿bajará conmigo a las puertas del Seol, o descender juntos al polvo?” (Sheol )
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol )