< Isaías 5 >
1 Déjenme cantar para mi bien amado una canción de mi amado sobre su viña. Mi amado tenía un viñedo en una colina muy fructífera.
Ndidzamuyimbira bwenzi langa nyimbo yokamba za munda wake wa mpesa: Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa pa phiri la nthaka yachonde.
2 Lo desenterró, recogió sus piedras, la plantó con la vid más selecta, construyó una torre en el centro, y también recortó una prensa de vino en ella. Buscó que diera uvas, pero dio uvas silvestres.
Anatipula nachotsa miyala yonse ndipo anawokamo mipesa yabwino kwambiri. Anamanga nsanja yolondera pakati pa mundawo ndipo anasemanso mopsinyira mphesa mʼmundamo. Ndipo iye anayembekezera kuti mundawo udzabala mphesa zabwino, koma ayi, unabala mphesa zosadya.
3 “Ahora, habitantes de Jerusalén y hombres de Judá, por favor, juzga entre mi viña y yo.
“Tsopano, inu amene mumakhala mu Yerusalemu ndi inu anthu a ku Yuda, weruzani pakati pa ine ndi munda wanga wa mpesawu.
4 ¿Qué más se puede hacer a mi viña que no haya hecho yo en ella? ¿Por qué, cuando busqué que diera uvas, dio uvas silvestres?
Kodi nʼchiyaninso china chimene ndikanachitira munda wanga wa mpesa kupambana chomwe ndawuchitira kale? Pamene ndinkayembekezera kuti udzabala mphesa zabwino, bwanji unabala mphesa zosadya?
5 Ahora te diré lo que haré con mi viña. Quitaré su seto y será devorado. Derribaré su muro, y será pisoteado.
Tsopano ndikuwuzani chimene ndidzawuchitire munda wanga wa mpesa: ndidzachotsa mpanda wake, ndipo mundawo udzawonongeka; ndidzagwetsa khoma lake, ndipo nyama zidzapondapondamo.
6 La convertiré en un páramo. No se podará ni se azadonará, pero le crecerán zarzas y espinas. También ordenaré a las nubes que no llueva sobre él”.
Ndidzawusandutsa tsala, udzakhala wosatengulira ndi wosalimira ndipo mudzamera mkandankhuku ndi minga ina. Ndidzalamula mitambo kuti isagwetse mvula pa mundapo.”
7 Porque la viña del Señor de los Ejércitos es la casa de Israel, y los hombres de Judá su planta agradable. Buscó la justicia, pero he aquí la opresión, por la justicia, pero he aquí un grito de angustia.
Munda wamphesa wa Yehova Wamphamvuzonse ndi Aisraeli, ndipo anthu a ku Yuda ndiwo minda yake yomukondweretsa. Ndipo Iye ankayembekezera chiweruzo cholungama, mʼmalo mwake anaona kuphana; mʼmalo mwa chilungamo Iye anamva kulira kwa anthu ozunzika.
8 Ay de los que se unen de casa en casa, que se acuestan campo a campo, hasta que no hay espacio, ¡y se te hace habitar solo en medio de la tierra!
Tsoka kwa inu amene mumangokhalira kulumikiza nyumba, ndipo mumangokhalira kuwonjezera minda, mpaka mutalanda malo onse kuti muzikhalamo nokha mʼdzikomo.
9 En mis oídos, el Señor de los Ejércitos dice: “Seguramente muchas casas quedarán desoladas, incluso grande y hermosa, desocupada.
Yehova Wamphamvuzonse wayankhula ine ndikumva kuti, “Ndithudi nyumba zambirizo zidzasanduka mabwinja, nyumba zazikulu zokongolazo zidzakhala zopanda anthu.
10 Por diez acres de viñedo se producirá un baño, y un homer de semilla dará un efa”.
Munda wamphesa wa maekala khumi udzatulutsa vinyo wodzaza mbiya imodzi, kufesa madengu khumi a mbewu, zokolola zake zidzangodzaza dengu limodzi.”
11 Ay de los que se levantan de madrugada para seguir la bebida fuerte, que se quedan hasta altas horas de la noche, ¡hasta que el vino los enardece!
Tsoka kwa iwo amene amadzuka mmamawa nathamangira chakumwa choledzeretsa, amene amamwa mpaka usiku kufikira ataledzera kotheratu.
12 El arpa, la lira, la pandereta y la flauta, con vino, están en sus fiestas; pero no respetan la obra de Yahvé, ni han considerado la operación de sus manos.
Pa maphwando awo pamakhala azeze, apangwe, matambolini, zitoliro ndi vinyo, ndipo sasamala ntchito za Yehova, salemekeza ntchito za manja ake.
13 Por eso mi pueblo va al cautiverio por falta de conocimiento. Sus honorables hombres están hambrientos, y sus multitudes están muertas de sed.
Motero anthu anga adzatengedwa ukapolo chifukwa cha kusamvetsa zinthu; atsogoleri awo olemekezeka adzafa ndi njala, ndipo anthu wamba ochuluka adzafa ndi ludzu.
14 Por lo tanto, el Seol ha ampliado su deseo, y abrió su boca sin medida; y su gloria, su multitud, su pompa, y el que se regocija entre ellos, descienden a ella. (Sheol )
Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake; mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka; adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko. (Sheol )
15 Así el hombre se rebaja, la humanidad es humilde, y los ojos de los arrogantes se humillan;
Ndipo munthu aliyense adzatsitsidwa, anthu onse adzachepetsedwa, anthu odzikuza adzachita manyazi.
16 pero Yahvé de los Ejércitos es exaltado en la justicia, y Dios el Santo es santificado en justicia.
Koma Yehova Wamphamvuzonse adzalemekezedwa chifukwa cha chiweruzo chake cholungama. Ndipo Mulungu woyera adzadzionetsa kuti ndi woyera pochita chilungamo chake.
17 Entonces los corderos pastarán como en su pasto, y los extraños comerán las ruinas de los ricos.
Tsono nkhosa zidzadya pamenepo ngati pabusa pawo; ana ankhosa adzadya mʼmabwinja a anthu olemera.
18 Ay de los que atraen la iniquidad con cuerdas de mentira, y la maldad como con cuerda de carreta,
Tsoka kwa amene amadzikokera tchimo ndi zingwe zachinyengo, ndipo amadzikokera zoyipa ndi zingwe zokokera ngolo,
19 que dicen: “Que se apresure, que acelere su obra, para que la veamos; que el consejo del Santo de Israel se acerque y venga, para que lo conozcamos”.
amene amanena kuti, “Yehova afulumire, agwire ntchito yake mwamsanga kuti ntchitoyo tiyione. Ntchito zionekere, zimene Woyerayo wa Israeli akufuna kuchita, zichitike kuti tizione.”
20 Ay de los que llaman bueno al mal y malo al bien; que puso la oscuridad por la luz, y la luz para la oscuridad; que puso lo amargo por lo dulce, ¡y dulce por amargo!
Tsoka kwa amene zoyipa amaziyesa zabwino ndipo zabwino amaziyesa zoyipa, amene mdima amawuyesa kuwala ndipo kuwala amakuyesa mdima, amene zowawasa amaziyesa zotsekemera ndipo zotsekemera amaziyesa zowawasa.
21 Ay de los que son sabios a sus propios ojos, ¡y prudente ante sus propios ojos!
Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeru ndipo amadziyesa ochenjera.
22 Ay de los que son poderosos para beber vino, y campeones en la mezcla de bebidas fuertes;
Tsoka kwa zidakwa zimene zimayika mtima pa vinyo ndipo ndi akatswiri posakaniza zakumwa,
23 que absuelven a los culpables a cambio de un soborno, ¡pero negar la justicia a los inocentes!
amene amamasula olakwa chifukwa cha chiphuphu koma amayipitsa mlandu wa munthu wosalakwa.
24 Por eso, como la lengua de fuego devora el rastrojo, y como la hierba seca se hunde en la llama, por lo que su raíz será como la podredumbre, y su flor se convertirá en polvo, porque han rechazado la ley de Yahvé de los Ejércitos, y despreciaron la palabra del Santo de Israel.
Nʼchifukwa chake monga momwe moto umawonongera chiputu ndipo monga momwe udzu wowuma umapsera mʼmalawi a moto, momwemonso mizu yawo idzawola ndipo maluwa awo adzafota ndi kuwuluka ngati fumbi; chifukwa akana malamulo a Yehova Wamphamvuzonse, ndipo anyoza mawu a Woyerayo wa Israeli.
25 Por eso la ira de Yahvé arde contra su pueblo, y ha extendido su mano contra ellos y los ha golpeado. Las montañas tiemblan, y sus cadáveres son como basura en medio de las calles. Por todo esto, su ira no se desvía, pero su mano sigue extendida.
Nʼchifukwa chake mkwiyo wa Yehova wayakira anthu ake; watambasula dzanja lake pa anthuwo ndipo akuwakantha Mapiri akugwedezeka, ndipo mitembo ya anthu yangoti mbwee mʼmisewu ngati zinyalala. Komabe ngakhale watero, mkwiyo wake sunaleke, dzanja lake likanali chitambasulire;
26 Él levantará un estandarte a las naciones desde muy lejos, y les silbará desde el fin de la tierra. He aquí que vendrán rápida y velozmente.
Yehova wakweza mbendera kuyitana mtundu wa anthu akutali, akuyitana anthuwo ndi likhweru kuti abwere kuchokera ku mathero a dziko lapansi. Awo akubwera, akubweradi mofulumira kwambiri!
27 Nadie se cansará ni tropezará entre ellos; nadie se adormecerá ni dormirá, ni se desatará el cinturón de su cintura, ni se rompa la correa de sus sandalias,
Palibe ndi mmodzi yemwe amene akutopa kapena kupunthwa, palibe amene akusinza kapena kugona; palibe lamba wa mʼchiwuno amene akumasuka, palibe chingwe cha nsapato chimene chaduka.
28 cuyas flechas son afiladas, y todos sus arcos doblados. Los cascos de sus caballos serán como el pedernal, y sus ruedas como un torbellino.
Mivi yawo ndi yakuthwa, mauta awo onse ndi okoka, ziboda za akavalo awo nʼzolimba ngati mwala wansagalabwi, magaleta awo ndi aliwiro ngati kamvuluvulu.
29 Su rugido será como el de una leona. Rugirán como jóvenes leones. Sí, rugirán, y agarrar su presa y llevársela, y no habrá nadie que lo entregue.
Kufuwula kwawo kuli ngati kubangula kwa mkango, amabangula ngati misona ya mkango; imadzuma pamene ikugwira nyama ndipo imapita nayo popanda ndi mmodzi yemwe woyipulumutsa.
30 En aquel día rugirán contra ellos como el rugido del mar. Si uno mira a la tierra, he aquí la oscuridad y la angustia. La luz se oscurece en sus nubes.
Tsiku limenelo mitundu ya anthu idzabangula ngati mkokomo wa madzi a mʼnyanja. Ndipo wina akakayangʼana dzikolo adzangoona mdima ndi zovuta; ngakhale kuwala kudzasanduka mdima chifukwa cha mitambo.