< Oseas 8 >

1 “¡Pon la trompeta en tus labios! Algo así como un águila está sobre la casa de Yahvé, porque han roto mi pacto y se rebelaron contra mi ley.
“Ika lipenga pakamwa pako. Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova chifukwa anthu aphwanya pangano langa ndiponso agalukira lamulo langa.
2 Me gritan: ‘¡Dios mío, nosotros, Israel, te reconocemos!
Israeli akulirira kwa Ine kuti, ‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
3 Israel ha abandonado lo que es bueno. El enemigo lo perseguirá.
Koma Israeli wakana zabwino; mdani adzamuthamangitsa.
4 Han puesto reyes, pero no por mí. Han hecho príncipes, y yo no lo he aprobado. De su plata y su oro se han hecho ídolos, para que sean cortados.
Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga. Amasankha akalonga popanda chilolezo changa. Amadzipangira mafano asiliva ndi agolide koma adzawonongeka nawo.
5 ¡Que Samaria arroje su ídolo del becerro! ¡Mi ira arde contra ellos! ¿Cuánto tiempo pasará hasta que sean capaces de la pureza?
Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe! Mkwiyo wanga wayakira anthuwo. Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
6 ¡Pues esto es incluso de Israel! El obrero lo hizo, y no es Dios; En efecto, el becerro de Samaria será despedazado.
Mafanowa ndi ochokera ku Israeli! Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso; si Mulungu amene anamupanga. Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa, mwana wangʼombe wa ku Samariya.
7 Porque ellos siembran el viento, y cosecharán el torbellino. No tiene grano en pie. El tallo no producirá ninguna cabeza. Si cede, los extraños se lo tragarán.
“Aisraeli amadzala mphepo ndipo amakolola kamvuluvulu. Tirigu alibe ngala; sadzabala chakudya. Akanabala chakudya alendo akanadya chakudyacho.
8 Israel es tragado. Ahora están entre las naciones como una cosa sin valor.
Israeli wamezedwa, tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina ngati chinthu cha chabechabe.
9 Porque han subido a Asiria, como un burro salvaje que vaga solo. Efraín ha contratado amantes para sí mismo.
Pakuti iwo anapita ku Asiriya ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha. Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
10 Pero aunque se vendieron entre las naciones, Ahora los reuniré; y comienzan a consumirse a causa de la opresión del rey de los poderosos.
Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu, Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi. Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.
11 Porque Efraín ha multiplicado los altares para pecar, se convirtieron para él en altares para pecar.
“Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo, maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
12 Le escribí las muchas cosas de mi ley, pero fueron considerados como algo extraño.
Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga, koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
13 En cuanto a los sacrificios de mis ofrendas, sacrifican carne y la comen, pero Yahvé no los acepta. Ahora se acordará de su iniquidad, y castigar sus pecados. Volverán a Egipto.
Amapereka nsembe za nyama kwa Ine ndipo iwo amadya nyamayo, koma Yehova sakondwera nazo. Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo: iwowo adzabwerera ku Igupto.
14 Porque Israel se ha olvidado de su Hacedor y ha construido palacios; y Judá ha multiplicado las ciudades fortificadas; pero yo enviaré un fuego sobre sus ciudades, y devorará sus fortalezas”.
Israeli wayiwala Mlengi wake ndipo wamanga nyumba zaufumu; Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga. Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo, moto umene udzatenthe malinga awo.”

< Oseas 8 >