< Éxodo 27 >

1 “Harás el altar de madera de acacia, de cinco codos de largo y cinco codos de ancho. El altar será cuadrado. Su altura será de tres codos.
“Upange guwa lansembe lamatabwa amtengo wa mkesha. Likhale lofanana mbali zonse, msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi mwake masentimita 229.
2 Harás sus cuernos en sus cuatro esquinas. Sus cuernos serán de una sola pieza con él. Lo cubrirás de bronce.
Upange nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo kuti nyangazo ndi guwalo zikhale chinthu chimodzi, ndipo ulikute guwalo ndi mkuwa.
3 Harás sus ollas para recoger sus cenizas, sus palas, sus cuencos, sus ganchos para la carne y sus sartenes para el fuego. Harás todos sus recipientes de bronce.
Upange ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika yochotsera phulusa, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
4 Le harás una rejilla de red de bronce. En la red harás cuatro anillos de bronce en sus cuatro esquinas.
Upange sefa yachitsulo chamkuwa ndipo mʼngodya zake zinayizo upangiremo mphete zamkuwa.
5 La pondrás debajo de la cornisa que rodea el altar, para que la red llegue hasta la mitad del altar.
Uyike sefayo mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, ndipo ilekezere pakati pa guwa lansembelo.
6 Harás varas para el altar, varas de madera de acacia, y las cubrirás de bronce.
Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndipo uzikutire ndi mkuwa.
7 Sus varas se pondrán en los anillos, y las varas estarán a los dos lados del altar cuando lo lleves.
Pamene mukunyamula guwalo, muzilowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo.
8 Lo harás hueco con tablas. Lo harán como se te ha mostrado en la montaña.
Guwalo likhale lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake. Ulipange monga momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
9 “Harás el atrio del tabernáculo: para el lado sur, hacia el sur, habrá cortinas para el atrio de lino fino de cien codos de largo por un lado.
“Upange bwalo la chihema. Mbali yakummwera ikhale yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
10 Sus columnas serán veinte, y sus bases veinte, de bronce. Los ganchos de las columnas y sus filetes serán de plata.
Upangenso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa, ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
11 Asimismo, para la longitud del lado norte, habrá cortinas de cien codos, y sus columnas serán veinte, y sus bases veinte, de bronce; los ganchos de las columnas y sus filetes, de plata.
Mbali yakumpoto ikhalenso yotalika mamita 46 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga. Pakhalenso mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
12 La anchura del atrio del lado occidental tendrá cortinas de cincuenta codos; sus columnas, diez, y sus basas, diez.
“Mbali yakumadzulo ya bwalolo ikhale yotalika mamita 23 ndipo ikhale ndi nsalu yotchinga, nsichi khumi ndi matsinde khumi.
13 La anchura del atrio del lado oriental será de cincuenta codos.
Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, kutalika kwa bwalo kukhale mamita 23.
14 Las cortinas de un lado de la puerta serán de quince codos, sus columnas de tres y sus bases de tres.
Mbali imodzi yachipata kukhale nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu.
15 Las cortinas del otro lado serán de quince codos; sus columnas, tres, y sus bases, tres.
Ndipo ku mbali inayo kukhale nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
16 Para la puerta del atrio habrá una cortina de veinte codos, de azul, púrpura, carmesí y lino torcido, obra del bordador; sus columnas cuatro, y sus bases cuatro.
“Pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotchinga yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira ndiponso yofewa yosalala. Nsaluyo ikhale yotalika mamita asanu ndi anayi, yopangidwa ndi anthu aluso. Pakhalenso mizati yake inayi ndi matsinde akenso anayi.
17 Todas las columnas del atrio alrededor estarán forradas de plata; sus ganchos, de plata, y sus bases, de bronce.
Mizati yonse yozungulira bwalolo ilumikizidwe ndi zingwe zasiliva. Ngowe zake zikhale zasiliva, koma matsinde ake akhale amkuwa.
18 La longitud del atrio será de cien codos, la anchura de cincuenta y la altura de cinco codos, de lino fino, y sus bases de bronce.
Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa.
19 Todos los instrumentos del tabernáculo en todo su servicio, y todos sus pasadores, y todos los pasadores del atrio, serán de bronce.
Zipangizo zonse zogwiritsa ntchito zosiyanasiyana pa chihemacho, zikhomo za chihema ndi zabwalolo zikhale zamkuwa.
20 “Mandarás a los hijos de Israel que te traigan aceite de oliva puro batido para la luz, para hacer arder continuamente una lámpara.
“Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
21 En la Tienda del Encuentro, fuera del velo que está delante del pacto, Aarón y sus hijos la mantendrán en orden desde la tarde hasta la mañana delante de Yahvé; será un estatuto para siempre a través de sus generaciones a favor de los hijos de Israel.
Mʼchihema cha msonkhano, koma kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, Aaroni ndi ana ake azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pakati pa Aisraeli pa mibado yonse.”

< Éxodo 27 >